Masalimo 140
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
140 Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
tetezeni kwa anthu ankhanza,
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
Sela
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
amene amakonza zokola mapazi anga.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
iwo atchera zingwe za maukonde awo
ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
Sela
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Imvani kupempha kwanga Yehova.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
musalole kuti zokonza zawo zitheke,
mwina iwo adzayamba kunyada.
Sela
9 Mitu ya amene andizungulira
iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Makala amoto agwere pa iwo;
aponyedwe pa moto,
mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
choyipa chilondole anthu ankhanza.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Psalm 140
New International Version
Psalm 140[a]
For the director of music. A psalm of David.
1 Rescue me,(A) Lord, from evildoers;
protect me from the violent,(B)
2 who devise evil plans(C) in their hearts
and stir up war(D) every day.
3 They make their tongues as sharp as(E) a serpent’s;
the poison of vipers(F) is on their lips.[b]
4 Keep me safe,(G) Lord, from the hands of the wicked;(H)
protect me from the violent,
who devise ways to trip my feet.
5 The arrogant have hidden a snare(I) for me;
they have spread out the cords of their net(J)
and have set traps(K) for me along my path.
6 I say to the Lord, “You are my God.”(L)
Hear, Lord, my cry for mercy.(M)
7 Sovereign Lord,(N) my strong deliverer,
you shield my head in the day of battle.
8 Do not grant the wicked(O) their desires, Lord;
do not let their plans succeed.
Footnotes
- Psalm 140:1 In Hebrew texts 140:1-13 is numbered 140:2-14.
- Psalm 140:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 5 and 8.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.