Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

140 Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
    tetezeni kwa anthu ankhanza,
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
    ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
    pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
            Sela

Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
    tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
    amene amakonza zokola mapazi anga.
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
    iwo atchera zingwe za maukonde awo
    ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
            Sela

Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
    Imvani kupempha kwanga Yehova.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
    mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
    musalole kuti zokonza zawo zitheke,
    mwina iwo adzayamba kunyada.
            Sela

Mitu ya amene andizungulira
    iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Makala amoto agwere pa iwo;
    aponyedwe pa moto,
    mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
    choyipa chilondole anthu ankhanza.

12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
    ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
    ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Psalm 140[a]

For the director of music. A psalm of David.

Rescue me,(A) Lord, from evildoers;
    protect me from the violent,(B)
who devise evil plans(C) in their hearts
    and stir up war(D) every day.
They make their tongues as sharp as(E) a serpent’s;
    the poison of vipers(F) is on their lips.[b]

Keep me safe,(G) Lord, from the hands of the wicked;(H)
    protect me from the violent,
    who devise ways to trip my feet.
The arrogant have hidden a snare(I) for me;
    they have spread out the cords of their net(J)
    and have set traps(K) for me along my path.

I say to the Lord, “You are my God.”(L)
    Hear, Lord, my cry for mercy.(M)
Sovereign Lord,(N) my strong deliverer,
    you shield my head in the day of battle.
Do not grant the wicked(O) their desires, Lord;
    do not let their plans succeed.

Those who surround me proudly rear their heads;
    may the mischief of their lips engulf them.(P)
10 May burning coals fall on them;
    may they be thrown into the fire,(Q)
    into miry pits, never to rise.
11 May slanderers not be established in the land;
    may disaster hunt down the violent.(R)

12 I know that the Lord secures justice for the poor(S)
    and upholds the cause(T) of the needy.(U)
13 Surely the righteous will praise your name,(V)
    and the upright will live(W) in your presence.(X)

Footnotes

  1. Psalm 140:1 In Hebrew texts 140:1-13 is numbered 140:2-14.
  2. Psalm 140:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 5 and 8.