Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

141 Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.
    Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;
    kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

Yehova ikani mlonda pakamwa panga;
    londerani khomo la pa milomo yanga.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;
    kuchita ntchito zonyansa
pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;
    musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;
    andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.
    Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
    Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,
    ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,
    ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;
    ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,
    ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,
    mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

Psalm 141

A psalm of David.

I call to you, Lord, come quickly(A) to me;
    hear me(B) when I call to you.
May my prayer be set before you like incense;(C)
    may the lifting up of my hands(D) be like the evening sacrifice.(E)

Set a guard over my mouth,(F) Lord;
    keep watch over the door of my lips.(G)
Do not let my heart(H) be drawn to what is evil
    so that I take part in wicked deeds(I)
along with those who are evildoers;
    do not let me eat their delicacies.(J)

Let a righteous man strike me—that is a kindness;
    let him rebuke me(K)—that is oil on my head.(L)
My head will not refuse it,
    for my prayer will still be against the deeds of evildoers.

Their rulers will be thrown down from the cliffs,(M)
    and the wicked will learn that my words were well spoken.
They will say, “As one plows(N) and breaks up the earth,(O)
    so our bones have been scattered at the mouth(P) of the grave.”

But my eyes are fixed(Q) on you, Sovereign Lord;
    in you I take refuge(R)—do not give me over to death.
Keep me safe(S) from the traps set by evildoers,(T)
    from the snares(U) they have laid for me.
10 Let the wicked fall(V) into their own nets,
    while I pass by in safety.(W)