Add parallel Print Page Options

147 Tamandani Yehova.

Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,
    nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!

Yehova akumanga Yerusalemu;
    Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Akutsogolera anthu osweka mtima
    ndi kumanga mabala awo.

Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,
    ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;
    nzeru zake zilibe malire.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,
    koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

Imbirani Yehova ndi mayamiko;
    imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;
    amapereka mvula ku dziko lapansi
    ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe
    ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.

10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,
    kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,
    amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.

12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;
    tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako
    ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako
    ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;
    mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya
    ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala.
    Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;
    amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,
    malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;
    anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Psalm 147

Praise the Lord.[a]

How good it is to sing praises to our God,
    how pleasant(A) and fitting to praise him!(B)

The Lord builds up Jerusalem;(C)
    he gathers the exiles(D) of Israel.
He heals the brokenhearted(E)
    and binds up their wounds.(F)
He determines the number of the stars(G)
    and calls them each by name.
Great is our Lord(H) and mighty in power;(I)
    his understanding has no limit.(J)
The Lord sustains the humble(K)
    but casts the wicked(L) to the ground.

Sing to the Lord(M) with grateful praise;(N)
    make music(O) to our God on the harp.(P)

He covers the sky with clouds;(Q)
    he supplies the earth with rain(R)
    and makes grass grow(S) on the hills.
He provides food(T) for the cattle
    and for the young ravens(U) when they call.

10 His pleasure is not in the strength(V) of the horse,(W)
    nor his delight in the legs of the warrior;
11 the Lord delights(X) in those who fear him,(Y)
    who put their hope(Z) in his unfailing love.(AA)

12 Extol the Lord, Jerusalem;(AB)
    praise your God, Zion.

13 He strengthens the bars of your gates(AC)
    and blesses your people(AD) within you.
14 He grants peace(AE) to your borders
    and satisfies you(AF) with the finest of wheat.(AG)

15 He sends his command(AH) to the earth;
    his word runs(AI) swiftly.
16 He spreads the snow(AJ) like wool
    and scatters the frost(AK) like ashes.
17 He hurls down his hail(AL) like pebbles.
    Who can withstand his icy blast?
18 He sends his word(AM) and melts them;
    he stirs up his breezes,(AN) and the waters flow.

19 He has revealed his word(AO) to Jacob,(AP)
    his laws and decrees(AQ) to Israel.
20 He has done this for no other nation;(AR)
    they do not know(AS) his laws.[b]

Praise the Lord.(AT)

Footnotes

  1. Psalm 147:1 Hebrew Hallelu Yah; also in verse 20
  2. Psalm 147:20 Masoretic Text; Dead Sea Scrolls and Septuagint nation; / he has not made his laws known to them