Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

15 Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?
    Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

Munthu wa makhalidwe abwino,
    amene amachita zolungama,
woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
    ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,
amene sachitira choyipa mnansi wake
    kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.
    Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,
amene amakwaniritsa zomwe walonjeza
    ngakhale pamene zikumupweteka,
amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja
    ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi
    sadzagwedezeka konse.

Psalm 15

A psalm of David.

Lord, who may dwell(A) in your sacred tent?(B)
    Who may live on your holy mountain?(C)

The one whose walk is blameless,(D)
    who does what is righteous,
    who speaks the truth(E) from their heart;
whose tongue utters no slander,(F)
    who does no wrong to a neighbor,
    and casts no slur on others;
who despises a vile person
    but honors(G) those who fear the Lord;
who keeps an oath(H) even when it hurts,
    and does not change their mind;
who lends money to the poor without interest;(I)
    who does not accept a bribe(J) against the innocent.

Whoever does these things
    will never be shaken.(K)