Add parallel Print Page Options

Pemphero la Davide.

17 Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;
    mverani kulira kwanga.
Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa
    popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;
    maso anu aone chimene ndi cholungama.

Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,
    ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;
    Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Kunena za ntchito za anthu,
    monga mwa mawu a pakamwa panu,
Ine ndadzisunga ndekha
    posatsata njira zachiwawa.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;
    mapazi anga sanaterereke.

Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;
    tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,
    Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja
    iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Mundisunge ine ngati mwanadiso;
    mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,
    kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,
    ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Andisaka, tsopano andizungulira
    ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;
    ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;
    landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,
    kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;
    ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,
    ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;
    pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Psalm 17

A prayer of David.

Hear me,(A) Lord, my plea is just;
    listen to my cry.(B)
Hear(C) my prayer—
    it does not rise from deceitful lips.(D)
Let my vindication(E) come from you;
    may your eyes see what is right.(F)

Though you probe my heart,(G)
    though you examine me at night and test me,(H)
you will find that I have planned no evil;(I)
    my mouth has not transgressed.(J)
Though people tried to bribe me,
    I have kept myself from the ways of the violent
    through what your lips have commanded.
My steps have held to your paths;(K)
    my feet have not stumbled.(L)

I call on you, my God, for you will answer me;(M)
    turn your ear to me(N) and hear my prayer.(O)
Show me the wonders of your great love,(P)
    you who save by your right hand(Q)
    those who take refuge(R) in you from their foes.
Keep me(S) as the apple of your eye;(T)
    hide me(U) in the shadow of your wings(V)
from the wicked who are out to destroy me,
    from my mortal enemies who surround me.(W)

10 They close up their callous hearts,(X)
    and their mouths speak with arrogance.(Y)
11 They have tracked me down, they now surround me,(Z)
    with eyes alert, to throw me to the ground.
12 They are like a lion(AA) hungry for prey,(AB)
    like a fierce lion crouching in cover.

13 Rise up,(AC) Lord, confront them, bring them down;(AD)
    with your sword rescue me from the wicked.
14 By your hand save me from such people, Lord,
    from those of this world(AE) whose reward is in this life.(AF)
May what you have stored up for the wicked fill their bellies;
    may their children gorge themselves on it,
    and may there be leftovers(AG) for their little ones.

15 As for me, I will be vindicated and will see your face;
    when I awake,(AH) I will be satisfied with seeing your likeness.(AI)