Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

19 Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;
    thambo limalalikira ntchito za manja ake.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,
    usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;
    liwu lawo silimveka.
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,
    mawuwo amafika mpaka
kumalekezero a dziko lapansi.
    Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,
    ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo
    ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;
    palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.

Lamulo la Yehova ndi langwiro,
    kutsitsimutsa moyo.
Maumboni a Yehova ndi odalirika,
    amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
Malangizo a Yehova ndi olungama,
    amapereka chimwemwe mu mtima.
Malamulo a Yehova ndi onyezimira,
    amapereka kuwala.
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,
    chimakhala mpaka muyaya.
Maweruzo a Yehova ndi owona
    ndipo onse ndi olungama;
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide,
    kuposa golide weniweni;
ndi otsekemera kuposa uchi,
    kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;
    powasunga pali mphotho yayikulu.

12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?
    Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;
    iwo asandilamulire.
Kotero ndidzakhala wosalakwa,
    wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga
    zikhale zokondweretsa pamaso panu,
    Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

Psalm 19[a]

For the director of music. A psalm of David.

The heavens(A) declare(B) the glory of God;(C)
    the skies(D) proclaim the work of his hands.(E)
Day after day they pour forth speech;
    night after night they reveal knowledge.(F)
They have no speech, they use no words;
    no sound is heard from them.
Yet their voice[b] goes out into all the earth,
    their words to the ends of the world.(G)
In the heavens God has pitched a tent(H) for the sun.(I)
    It is like a bridegroom(J) coming out of his chamber,(K)
    like a champion(L) rejoicing to run his course.
It rises at one end of the heavens(M)
    and makes its circuit to the other;(N)
    nothing is deprived of its warmth.

The law of the Lord(O) is perfect,(P)
    refreshing the soul.(Q)
The statutes of the Lord are trustworthy,(R)
    making wise the simple.(S)
The precepts of the Lord are right,(T)
    giving joy(U) to the heart.
The commands of the Lord are radiant,
    giving light to the eyes.(V)
The fear of the Lord(W) is pure,
    enduring forever.
The decrees of the Lord are firm,
    and all of them are righteous.(X)

10 They are more precious than gold,(Y)
    than much pure gold;
they are sweeter than honey,(Z)
    than honey from the honeycomb.(AA)
11 By them your servant is warned;
    in keeping them there is great reward.
12 But who can discern their own errors?
    Forgive my hidden faults.(AB)
13 Keep your servant also from willful sins;(AC)
    may they not rule over me.(AD)
Then I will be blameless,(AE)
    innocent of great transgression.

14 May these words of my mouth and this meditation of my heart
    be pleasing(AF) in your sight,
    Lord, my Rock(AG) and my Redeemer.(AH)

Footnotes

  1. Psalm 19:1 In Hebrew texts 19:1-14 is numbered 19:2-15.
  2. Psalm 19:4 Septuagint, Jerome and Syriac; Hebrew measuring line