Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

40 Mofatsa ndinadikira Yehova
    Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,
    mʼthope ndi mʼchithaphwi;
Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe
    ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,
    nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.
Ambiri adzaona,
    nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

Ndi wodala munthu
    amakhulupirira Yehova;
amene sayembekezera kwa odzikuza,
    kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Zambiri, Yehova Mulungu wanga,
    ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.
Zinthu zimene munazikonzera ife
    palibe amene angathe kukuwerengerani.
Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,
    zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,
    koma makutu anga mwawatsekula;
zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo
    Inu simunazipemphe.
Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.
    Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;
    lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;
    sinditseka milomo yanga
    monga mukudziwa Inu Yehova.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;
    ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.
Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu
    pa msonkhano waukulu.

11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova;
    chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;
    machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.
Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,
    ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13 Pulumutseni Yehova;
    Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga
    achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene amakhumba chiwonongeko changa
    abwezedwe mwamanyazi.
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”
    abwerere akuchita manyazi.
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu
    akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
    nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;
    Ambuye andiganizire.
Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;
    Inu Mulungu wanga, musachedwe.

Psalm 40[a](A)

For the director of music. Of David. A psalm.

I waited patiently(B) for the Lord;
    he turned to me and heard my cry.(C)
He lifted me out of the slimy pit,(D)
    out of the mud(E) and mire;(F)
he set my feet(G) on a rock(H)
    and gave me a firm place to stand.
He put a new song(I) in my mouth,
    a hymn of praise to our God.
Many will see and fear the Lord(J)
    and put their trust(K) in him.

Blessed is the one(L)
    who trusts in the Lord,(M)
who does not look to the proud,(N)
    to those who turn aside to false gods.[b](O)
Many, Lord my God,
    are the wonders(P) you have done,
    the things you planned for us.
None can compare(Q) with you;
    were I to speak and tell of your deeds,
    they would be too many(R) to declare.

Sacrifice and offering you did not desire—(S)
    but my ears you have opened[c](T)
    burnt offerings(U) and sin offerings[d] you did not require.
Then I said, “Here I am, I have come—
    it is written about me in the scroll.[e](V)
I desire to do your will,(W) my God;(X)
    your law is within my heart.”(Y)

I proclaim your saving acts(Z) in the great assembly;(AA)
    I do not seal my lips, Lord,
    as you know.(AB)
10 I do not hide your righteousness in my heart;
    I speak of your faithfulness(AC) and your saving help.
I do not conceal your love and your faithfulness
    from the great assembly.(AD)

11 Do not withhold your mercy(AE) from me, Lord;
    may your love(AF) and faithfulness(AG) always protect(AH) me.
12 For troubles(AI) without number surround me;
    my sins have overtaken me, and I cannot see.(AJ)
They are more than the hairs of my head,(AK)
    and my heart fails(AL) within me.
13 Be pleased to save me, Lord;
    come quickly, Lord, to help me.(AM)

14 May all who want to take my life(AN)
    be put to shame and confusion;(AO)
may all who desire my ruin(AP)
    be turned back in disgrace.
15 May those who say to me, “Aha! Aha!”(AQ)
    be appalled at their own shame.
16 But may all who seek you(AR)
    rejoice and be glad(AS) in you;
may those who long for your saving help always say,
    “The Lord is great!”(AT)

17 But as for me, I am poor and needy;(AU)
    may the Lord think(AV) of me.
You are my help(AW) and my deliverer;(AX)
    you are my God, do not delay.(AY)

Footnotes

  1. Psalm 40:1 In Hebrew texts 40:1-17 is numbered 40:2-18.
  2. Psalm 40:4 Or to lies
  3. Psalm 40:6 Hebrew; some Septuagint manuscripts but a body you have prepared for me
  4. Psalm 40:6 Or purification offerings
  5. Psalm 40:7 Or come / with the scroll written for me