Add parallel Print Page Options

43 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;
    ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;
    mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.
    Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
    woponderezedwa ndi mdani?
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu
    kuti zinditsogolere;
mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,
    kumalo kumene inu mumakhala.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,
    kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.
Ndidzakutamandani ndi zeze,
    Inu Mulungu wanga.

Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?
    Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Khulupirira Mulungu,
    pakuti ndidzamutamandabe Iye,
    Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

Psalm 43[a]

Vindicate me, my God,
    and plead my cause(A)
    against an unfaithful nation.
Rescue me(B) from those who are
    deceitful and wicked.(C)
You are God my stronghold.
    Why have you rejected(D) me?
Why must I go about mourning,(E)
    oppressed by the enemy?(F)
Send me your light(G) and your faithful care,(H)
    let them lead me;(I)
let them bring me to your holy mountain,(J)
    to the place where you dwell.(K)
Then I will go(L) to the altar(M) of God,
    to God, my joy(N) and my delight.(O)
I will praise you with the lyre,(P)
    O God, my God.

Why, my soul, are you downcast?
    Why so disturbed within me?
Put your hope in God,
    for I will yet praise him,
    my Savior and my God.(Q)

Footnotes

  1. Psalm 43:1 In many Hebrew manuscripts Psalms 42 and 43 constitute one psalm.