Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

45 Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma
    pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;
    lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse
    ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,
    popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;
    mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso
    mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;
    dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,
    mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;
    ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
    choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu
    pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;
    kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu
    nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;
    ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;
    iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;
    mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,
    amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,
    chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;
    anamwali okhala naye akumutsatira
    ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;
    akulowa mʼnyumba yaufumu.

16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;
    udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;
    choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

Psalm 45[a]

For the director of music. To the tune of “Lilies.” Of the Sons of Korah. A maskil.[b] A wedding song.(A)

My heart is stirred by a noble theme
    as I recite my verses for the king;
    my tongue is the pen of a skillful writer.

You are the most excellent of men
    and your lips have been anointed with grace,(B)
    since God has blessed you forever.(C)

Gird your sword(D) on your side, you mighty one;(E)
    clothe yourself with splendor and majesty.(F)
In your majesty ride forth victoriously(G)
    in the cause of truth, humility and justice;(H)
    let your right hand(I) achieve awesome deeds.(J)
Let your sharp arrows(K) pierce the hearts(L) of the king’s enemies;(M)
    let the nations fall beneath your feet.
Your throne, O God,[c] will last for ever and ever;(N)
    a scepter of justice will be the scepter of your kingdom.
You love righteousness(O) and hate wickedness;(P)
    therefore God, your God, has set you above your companions
    by anointing(Q) you with the oil of joy.(R)
All your robes are fragrant(S) with myrrh(T) and aloes(U) and cassia;(V)
    from palaces adorned with ivory(W)
    the music of the strings(X) makes you glad.
Daughters of kings(Y) are among your honored women;
    at your right hand(Z) is the royal bride(AA) in gold of Ophir.(AB)

10 Listen, daughter,(AC) and pay careful attention:(AD)
    Forget your people(AE) and your father’s house.
11 Let the king be enthralled by your beauty;(AF)
    honor(AG) him, for he is your lord.(AH)
12 The city of Tyre(AI) will come with a gift,[d](AJ)
    people of wealth will seek your favor.
13 All glorious(AK) is the princess within her chamber;
    her gown is interwoven with gold.(AL)
14 In embroidered garments(AM) she is led to the king;(AN)
    her virgin companions(AO) follow her—
    those brought to be with her.
15 Led in with joy and gladness,(AP)
    they enter the palace of the king.

16 Your sons will take the place of your fathers;
    you will make them princes(AQ) throughout the land.

17 I will perpetuate your memory through all generations;(AR)
    therefore the nations will praise you(AS) for ever and ever.(AT)

Footnotes

  1. Psalm 45:1 In Hebrew texts 45:1-17 is numbered 45:2-18.
  2. Psalm 45:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 45:6 Here the king is addressed as God’s representative.
  4. Psalm 45:12 Or A Tyrian robe is among the gifts