Add parallel Print Page Options

Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

48 Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando
    mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Lokongola mu utali mwake,
    chimwemwe cha dziko lonse lapansi.
Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni,
    mzinda wa Mfumu yayikulu.
Mulungu ali mu malinga ake;
    Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.

Pamene mafumu anasonkhana pamodzi,
    pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri;
    anathawa ndi mantha aakulu.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera,
    ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi
    zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.

Monga momwe tinamvera,
    kotero ife tinaona
mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse,
    mu mzinda wa Mulungu wathu.
    Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.

Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,
    ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu,
    matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi
    dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera,
    midzi ya Yuda ndi yosangalala
    chifukwa cha maweruzo anu.

12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo,
    werengani nsanja zake.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake,
    penyetsetsani malinga ake,
    kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha;
    Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

Psalm 48[a]

A song. A psalm of the Sons of Korah.

Great is the Lord,(A) and most worthy of praise,(B)
    in the city of our God,(C) his holy mountain.(D)

Beautiful(E) in its loftiness,
    the joy of the whole earth,
like the heights of Zaphon[b](F) is Mount Zion,(G)
    the city of the Great King.(H)
God is in her citadels;(I)
    he has shown himself to be her fortress.(J)

When the kings joined forces,
    when they advanced together,(K)
they saw her and were astounded;
    they fled in terror.(L)
Trembling seized(M) them there,
    pain like that of a woman in labor.(N)
You destroyed them like ships of Tarshish(O)
    shattered by an east wind.(P)

As we have heard,
    so we have seen
in the city of the Lord Almighty,
    in the city of our God:
God makes her secure
    forever.[c](Q)

Within your temple, O God,
    we meditate(R) on your unfailing love.(S)
10 Like your name,(T) O God,
    your praise reaches to the ends of the earth;(U)
    your right hand is filled with righteousness.
11 Mount Zion rejoices,
    the villages of Judah are glad
    because of your judgments.(V)

12 Walk about Zion, go around her,
    count her towers,(W)
13 consider well her ramparts,(X)
    view her citadels,(Y)
that you may tell of them
    to the next generation.(Z)

14 For this God is our God for ever and ever;
    he will be our guide(AA) even to the end.

Footnotes

  1. Psalm 48:1 In Hebrew texts 48:1-14 is numbered 48:2-15.
  2. Psalm 48:2 Zaphon was the most sacred mountain of the Canaanites.
  3. Psalm 48:8 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.