Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.

51 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,
    molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
molingana ndi chifundo chanu chachikulu
    mufafanize mphulupulu zanga.
Munditsuke zolakwa zanga zonse
    ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.

Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,
    ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa
    ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,
Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama
    pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,
    wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;
    mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.

Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,
    munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,
    mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Mufulatire machimo anga
    ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.

10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu
    ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Musandichotse pamaso panu
    kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu
    ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.

13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu
    kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,
    Mulungu wa chipulumutso changa,
    ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,
    ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.
    Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;
    mtima wosweka ndi wachisoni
    Inu Mulungu simudzawunyoza.

18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;
    mumange makoma a Yerusalemu.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,
    nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;
    ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

Psalm 51[a]

For the director of music. A psalm of David. When the prophet Nathan came to him after David had committed adultery with Bathsheba.(A)

Have mercy(B) on me, O God,
    according to your unfailing love;(C)
according to your great compassion(D)
    blot out(E) my transgressions.(F)
Wash away(G) all my iniquity
    and cleanse(H) me from my sin.

For I know my transgressions,
    and my sin is always before me.(I)
Against you, you only, have I sinned(J)
    and done what is evil in your sight;(K)
so you are right in your verdict
    and justified when you judge.(L)
Surely I was sinful(M) at birth,(N)
    sinful from the time my mother conceived me.
Yet you desired faithfulness even in the womb;
    you taught me wisdom(O) in that secret place.(P)

Cleanse(Q) me with hyssop,(R) and I will be clean;
    wash me, and I will be whiter than snow.(S)
Let me hear joy and gladness;(T)
    let the bones(U) you have crushed rejoice.
Hide your face from my sins(V)
    and blot out(W) all my iniquity.

10 Create in me a pure heart,(X) O God,
    and renew a steadfast spirit within me.(Y)
11 Do not cast me(Z) from your presence(AA)
    or take your Holy Spirit(AB) from me.
12 Restore to me the joy of your salvation(AC)
    and grant me a willing spirit,(AD) to sustain me.(AE)

13 Then I will teach transgressors your ways,(AF)
    so that sinners(AG) will turn back to you.(AH)
14 Deliver me(AI) from the guilt of bloodshed,(AJ) O God,
    you who are God my Savior,(AK)
    and my tongue will sing of your righteousness.(AL)
15 Open my lips, Lord,(AM)
    and my mouth will declare your praise.
16 You do not delight in sacrifice,(AN) or I would bring it;
    you do not take pleasure in burnt offerings.
17 My sacrifice,(AO) O God, is[b] a broken spirit;
    a broken and contrite heart(AP)
    you, God, will not despise.

18 May it please you to prosper Zion,(AQ)
    to build up the walls of Jerusalem.(AR)
19 Then you will delight in the sacrifices of the righteous,(AS)
    in burnt offerings(AT) offered whole;
    then bulls(AU) will be offered on your altar.

Footnotes

  1. Psalm 51:1 In Hebrew texts 51:1-19 is numbered 51:3-21.
  2. Psalm 51:17 Or The sacrifices of God are