Masalimo 54
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”
54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Alendo akundithira nkhondo;
anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
pakuti ndi labwino.
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Psalm 54
New International Version
Psalm 54[a]
For the director of music. With stringed instruments. A maskil[b] of David. When the Ziphites(A) had gone to Saul and said, “Is not David hiding among us?”
1 Save me(B), O God, by your name;(C)
vindicate me by your might.(D)
2 Hear my prayer, O God;(E)
listen to the words of my mouth.
Footnotes
- Psalm 54:1 In Hebrew texts 54:1-7 is numbered 54:3-9.
- Psalm 54:1 Title: Probably a literary or musical term
- Psalm 54:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.