Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
    onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
    mvetserani mawu a pakamwa panga.

Alendo akundithira nkhondo;
    anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
    anthu amene salabadira za Mulungu.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
    Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
    mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
    ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
    pakuti ndi labwino.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
    ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

Psalm 54[a]

For the director of music. With stringed instruments. A maskil[b] of David. When the Ziphites(A) had gone to Saul and said, “Is not David hiding among us?”

Save me(B), O God, by your name;(C)
    vindicate me by your might.(D)
Hear my prayer, O God;(E)
    listen to the words of my mouth.

Arrogant foes are attacking me;(F)
    ruthless people(G) are trying to kill me(H)
    people without regard for God.[c](I)

Surely God is my help;(J)
    the Lord is the one who sustains me.(K)

Let evil recoil(L) on those who slander me;
    in your faithfulness(M) destroy them.

I will sacrifice a freewill offering(N) to you;
    I will praise(O) your name, Lord, for it is good.(P)
You have delivered me(Q) from all my troubles,
    and my eyes have looked in triumph on my foes.(R)

Footnotes

  1. Psalm 54:1 In Hebrew texts 54:1-7 is numbered 54:3-9.
  2. Psalm 54:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 54:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.