Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide.

Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,
    kapena kundilanga mu ukali wanu.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka;
    Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu.
    Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse;
    pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira;
    Amakutamandani ndani ali ku manda?

Ine ndatopa ndi kubuwula;
    usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga;
    ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni;
    akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa,
    pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo;
    Yehova walandira pemphero langa.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha;
    adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

Psalm 6[a]

For the director of music. With stringed instruments. According to sheminith.[b] A psalm of David.

Lord, do not rebuke me in your anger(A)
    or discipline me in your wrath.
Have mercy on me,(B) Lord, for I am faint;(C)
    heal me,(D) Lord, for my bones are in agony.(E)
My soul is in deep anguish.(F)
    How long,(G) Lord, how long?

Turn,(H) Lord, and deliver me;
    save me because of your unfailing love.(I)
Among the dead no one proclaims your name.
    Who praises you from the grave?(J)

I am worn out(K) from my groaning.(L)

All night long I flood my bed with weeping(M)
    and drench my couch with tears.(N)
My eyes grow weak(O) with sorrow;
    they fail because of all my foes.

Away from me,(P) all you who do evil,(Q)
    for the Lord has heard my weeping.
The Lord has heard my cry for mercy;(R)
    the Lord accepts my prayer.
10 All my enemies will be overwhelmed with shame and anguish;(S)
    they will turn back and suddenly be put to shame.(T)

Footnotes

  1. Psalm 6:1 In Hebrew texts 6:1-10 is numbered 6:2-11.
  2. Psalm 6:1 Title: Probably a musical term