Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

61 Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;
    mvetserani pemphero langa.

Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu
    ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;
    tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,
    nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya
    ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;
    mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,
    zaka zake kwa mibado yochuluka.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;
    ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu
    ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

Psalm 61[a]

For the director of music. With stringed instruments. Of David.

Hear my cry, O God;(A)
    listen to my prayer.(B)

From the ends of the earth I call to you,
    I call as my heart grows faint;(C)
    lead me to the rock(D) that is higher than I.
For you have been my refuge,(E)
    a strong tower against the foe.(F)

I long to dwell(G) in your tent forever
    and take refuge in the shelter of your wings.[b](H)
For you, God, have heard my vows;(I)
    you have given me the heritage of those who fear your name.(J)

Increase the days of the king’s life,(K)
    his years for many generations.(L)
May he be enthroned in God’s presence forever;(M)
    appoint your love and faithfulness to protect him.(N)

Then I will ever sing in praise of your name(O)
    and fulfill my vows day after day.(P)

Footnotes

  1. Psalm 61:1 In Hebrew texts 61:1-8 is numbered 61:2-9.
  2. Psalm 61:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.