Add parallel Print Page Options

Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.

Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
    pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
mwina angandikadzule ngati mkango,
    ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.

Inu Yehova Mulungu wanga,
    ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
    kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
    lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
    ndipo mundigoneke pa fumbi.
            Sela

Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
    nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
    Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
    Alamulireni muli kumwambako;
    Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
    monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Inu Mulungu wolungama,
    amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
    ndipo wolungama akhale motetezedwa.

10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
    amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
    Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
    Mulungu adzanola lupanga lake,
    Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
    Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.

14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
    Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
    amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
    chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.

17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
    ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

Psalm 7[a]

A shiggaion[b](A) of David, which he sang to the Lord concerning Cush, a Benjamite.

Lord my God, I take refuge(B) in you;
    save and deliver me(C) from all who pursue me,(D)
or they will tear me apart like a lion(E)
    and rip me to pieces with no one to rescue(F) me.

Lord my God, if I have done this
    and there is guilt on my hands(G)
if I have repaid my ally with evil
    or without cause(H) have robbed my foe—
then let my enemy pursue and overtake(I) me;
    let him trample my life to the ground(J)
    and make me sleep in the dust.[c](K)

Arise,(L) Lord, in your anger;
    rise up against the rage of my enemies.(M)
    Awake,(N) my God; decree justice.
Let the assembled peoples gather around you,
    while you sit enthroned over them on high.(O)
    Let the Lord judge(P) the peoples.
Vindicate me, Lord, according to my righteousness,(Q)
    according to my integrity,(R) O Most High.(S)
Bring to an end the violence of the wicked
    and make the righteous secure—(T)
you, the righteous God(U)
    who probes minds and hearts.(V)

10 My shield[d](W) is God Most High,
    who saves the upright in heart.(X)
11 God is a righteous judge,(Y)
    a God who displays his wrath(Z) every day.
12 If he does not relent,(AA)
    he[e] will sharpen his sword;(AB)
    he will bend and string his bow.(AC)
13 He has prepared his deadly weapons;
    he makes ready his flaming arrows.(AD)

14 Whoever is pregnant with evil
    conceives trouble and gives birth(AE) to disillusionment.
15 Whoever digs a hole and scoops it out
    falls into the pit(AF) they have made.(AG)
16 The trouble they cause recoils on them;
    their violence comes down on their own heads.

17 I will give thanks to the Lord because of his righteousness;(AH)
    I will sing the praises(AI) of the name of the Lord Most High.(AJ)

Footnotes

  1. Psalm 7:1 In Hebrew texts 7:1-17 is numbered 7:2-18.
  2. Psalm 7:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 7:5 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
  4. Psalm 7:10 Or sovereign
  5. Psalm 7:12 Or If anyone does not repent, / God