Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho.

70 Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;
    Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga
    achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene akukhumba chiwonongeko changa
    abwezedwe mopanda ulemu.
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”
    abwerere chifukwa cha manyazi awo.
Koma onse amene akufunafuna Inu
    akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
    nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”

Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;
    bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;
    Inu Yehova musachedwe.

Psalm 70[a](A)

For the director of music. Of David. A petition.

Hasten, O God, to save me;
    come quickly, Lord, to help me.(B)

May those who want to take my life(C)
    be put to shame and confusion;
may all who desire my ruin
    be turned back in disgrace.(D)
May those who say to me, “Aha! Aha!”(E)
    turn back because of their shame.
But may all who seek you(F)
    rejoice and be glad(G) in you;
may those who long for your saving help always say,
    “The Lord is great!”(H)

But as for me, I am poor and needy;(I)
    come quickly to me,(J) O God.
You are my help(K) and my deliverer;(L)
    Lord, do not delay.(M)

Footnotes

  1. Psalm 70:1 In Hebrew texts 70:1-5 is numbered 70:2-6.