Masalimo 70
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho.
70 Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;
Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene akukhumba chiwonongeko changa
abwezedwe mopanda ulemu.
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”
abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Koma onse amene akufunafuna Inu
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;
bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;
Inu Yehova musachedwe.
Psalm 70
New International Version
Psalm 70[a](A)
For the director of music. Of David. A petition.
1 Hasten, O God, to save me;
come quickly, Lord, to help me.(B)
2 May those who want to take my life(C)
be put to shame and confusion;
may all who desire my ruin
be turned back in disgrace.(D)
3 May those who say to me, “Aha! Aha!”(E)
turn back because of their shame.
4 But may all who seek you(F)
rejoice and be glad(G) in you;
may those who long for your saving help always say,
“The Lord is great!”(H)
Footnotes
- Psalm 70:1 In Hebrew texts 70:1-5 is numbered 70:2-6.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.