Add parallel Print Page Options

Salimo la Solomoni.

72 Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,
    Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,
    anthu anu ozunzika mosakondera.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,
    timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu
    ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;
    adzaphwanya ozunza anzawo.

Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,
    nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa
    ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;
    chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.

Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina
    ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake
    ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali
    adzabweretsa mitulo kwa iye,
mafumu a ku Seba ndi Seba
    adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Mafumu onse adzamuweramira
    ndipo mitundu yonse idzamutumikira.

12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,
    wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa
    ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa
    pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.

15 Iye akhale ndi moyo wautali;
    golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye.
Anthu amupempherere nthawi zonse
    ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;
    pamwamba pa mapiri pakhale tirigu.
Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni;
    zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya,
    lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa.

Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye
    ndipo iwo adzamutcha iye wodala.

18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli
    amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya
    dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.
            Ameni ndi Ameni.

20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

Psalm 72

Of Solomon.

Endow the king with your justice,(A) O God,
    the royal son with your righteousness.
May he judge your people in righteousness,(B)
    your afflicted ones with justice.

May the mountains bring prosperity to the people,
    the hills the fruit of righteousness.
May he defend the afflicted(C) among the people
    and save the children of the needy;(D)
    may he crush the oppressor.(E)
May he endure[a](F) as long as the sun,
    as long as the moon, through all generations.(G)
May he be like rain(H) falling on a mown field,
    like showers watering the earth.
In his days may the righteous flourish(I)
    and prosperity abound till the moon is no more.

May he rule from sea to sea
    and from the River[b](J) to the ends of the earth.(K)
May the desert tribes bow before him
    and his enemies lick the dust.
10 May the kings of Tarshish(L) and of distant shores(M)
    bring tribute to him.
May the kings of Sheba(N) and Seba
    present him gifts.(O)
11 May all kings bow down(P) to him
    and all nations serve(Q) him.

12 For he will deliver the needy who cry out,
    the afflicted who have no one to help.
13 He will take pity(R) on the weak and the needy
    and save the needy from death.
14 He will rescue(S) them from oppression and violence,
    for precious(T) is their blood in his sight.

15 Long may he live!
    May gold from Sheba(U) be given him.
May people ever pray for him
    and bless him all day long.(V)
16 May grain(W) abound throughout the land;
    on the tops of the hills may it sway.
May the crops(X) flourish like Lebanon(Y)
    and thrive[c] like the grass of the field.(Z)
17 May his name endure forever;(AA)
    may it continue as long as the sun.(AB)

Then all nations will be blessed through him,[d]
    and they will call him blessed.(AC)

18 Praise be to the Lord God, the God of Israel,(AD)
    who alone does marvelous deeds.(AE)
19 Praise be to his glorious name(AF) forever;
    may the whole earth be filled with his glory.(AG)
Amen and Amen.(AH)

20 This concludes the prayers of David son of Jesse.(AI)

Footnotes

  1. Psalm 72:5 Septuagint; Hebrew You will be feared
  2. Psalm 72:8 That is, the Euphrates
  3. Psalm 72:16 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text Lebanon, / from the city
  4. Psalm 72:17 Or will use his name in blessings (see Gen. 48:20)