Add parallel Print Page Options

Ndakatulo ya Asafu.

74 Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?
    Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,
    fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,
    phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya
    chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.

Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;
    anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo
    kuti adule mitengo mʼnkhalango.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo
    zonse zimene tinapachika.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;
    anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”
    Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;
    palibe aneneri amene atsala
    ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.

10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?
    Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?
    Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!

12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;
    Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;
    munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani
    ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,
    munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;
    Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;
    munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,
    momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;
    nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko
    asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;
    osauka ndi osowa atamande dzina lanu.

22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;
    kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,
    chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

Psalm 74

A maskil[a] of Asaph.

O God, why have you rejected(A) us forever?(B)
    Why does your anger smolder against the sheep of your pasture?(C)
Remember the nation you purchased(D) long ago,(E)
    the people of your inheritance,(F) whom you redeemed(G)
    Mount Zion,(H) where you dwelt.(I)
Turn your steps toward these everlasting ruins,(J)
    all this destruction the enemy has brought on the sanctuary.

Your foes roared(K) in the place where you met with us;
    they set up their standards(L) as signs.
They behaved like men wielding axes
    to cut through a thicket of trees.(M)
They smashed all the carved(N) paneling
    with their axes and hatchets.
They burned your sanctuary to the ground;
    they defiled(O) the dwelling place(P) of your Name.(Q)
They said in their hearts, “We will crush(R) them completely!”
    They burned(S) every place where God was worshiped in the land.

We are given no signs from God;(T)
    no prophets(U) are left,
    and none of us knows how long this will be.
10 How long(V) will the enemy mock(W) you, God?
    Will the foe revile(X) your name forever?
11 Why do you hold back your hand, your right hand?(Y)
    Take it from the folds of your garment(Z) and destroy them!

12 But God is my King(AA) from long ago;
    he brings salvation(AB) on the earth.

13 It was you who split open the sea(AC) by your power;
    you broke the heads of the monster(AD) in the waters.
14 It was you who crushed the heads of Leviathan(AE)
    and gave it as food to the creatures of the desert.(AF)
15 It was you who opened up springs(AG) and streams;
    you dried up(AH) the ever-flowing rivers.
16 The day is yours, and yours also the night;
    you established the sun and moon.(AI)
17 It was you who set all the boundaries(AJ) of the earth;
    you made both summer and winter.(AK)

18 Remember how the enemy has mocked you, Lord,
    how foolish people(AL) have reviled your name.
19 Do not hand over the life of your dove(AM) to wild beasts;
    do not forget the lives of your afflicted(AN) people forever.
20 Have regard for your covenant,(AO)
    because haunts of violence fill the dark places(AP) of the land.
21 Do not let the oppressed(AQ) retreat in disgrace;
    may the poor and needy(AR) praise your name.
22 Rise up,(AS) O God, and defend your cause;
    remember how fools(AT) mock you all day long.
23 Do not ignore the clamor(AU) of your adversaries,(AV)
    the uproar(AW) of your enemies,(AX) which rises continually.

Footnotes

  1. Psalm 74:1 Title: Probably a literary or musical term