Masalimo 82
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Asafu.
82 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Psalm 82
New International Version
Psalm 82
A psalm of Asaph.
2 “How long will you[a] defend the unjust
and show partiality(C) to the wicked?[b](D)
3 Defend the weak and the fatherless;(E)
uphold the cause of the poor(F) and the oppressed.
4 Rescue the weak and the needy;
deliver them from the hand of the wicked.
5 “The ‘gods’ know nothing, they understand nothing.(G)
They walk about in darkness;(H)
all the foundations(I) of the earth are shaken.
Footnotes
- Psalm 82:2 The Hebrew is plural.
- Psalm 82:2 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.