Add parallel Print Page Options

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

89 Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;
    ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,
    kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,
    ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.
    Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”
            Sela.

Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,
    kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?
    Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;
    Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?
    Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;
    pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
10 Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;
    ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
11 Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;
    munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
12 Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;
    Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
13 Mkono wanu ndi wamphamvu;
    dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14 Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;
    chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
15 Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,
    amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
16 Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;
    amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
17 Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo
    ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
18 Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,
    Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19 Kale munayankhula mʼmasomphenya,
    kwa anthu anu okhulupirika munati,
“Ndapatsa mphamvu wankhondo;
    ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
20 Ndamupeza mtumiki wanga Davide;
    ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
21 Dzanja langa lidzamuchirikiza;
    zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
22 Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;
    anthu oyipa sadzamusautsa.
23 Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake
    ndi kukantha otsutsana naye.
24 Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,
    ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
25 Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,
    dzanja lake lamanja pa mitsinje.
26 Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,
    Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
27 Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;
    wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
28 Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,
    ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
29 Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,
    mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30 “Ngati ana ake adzataya lamulo langa
    ndi kusatsatira malangizo anga,
31 ngati adzaswa malamulo anga
    ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
32 Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,
    mphulupulu zawo powakwapula.
33 Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,
    kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
34 Sindidzaswa pangano langa
    kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
35 Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga
    ndipo sindidzanama kwa Davide,
36 kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya
    ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
37 udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,
    mboni yokhulupirika mʼmitambo.
            Sela

38 “Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,
    mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
39 Mwakana pangano ndi mtumiki wanu
    ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
40 Inu mwagumula makoma ake onse
    ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
41 Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;
    iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
42 Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;
    mwachititsa kuti adani ake akondwere.
43 Mwabunthitsa lupanga lake,
    simunamuthandize pa nkhondo.
44 Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake
    ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
45 Mwachepetsa masiku a unyamata wake;
    mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.
            Sela

46 “Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?
    Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
47 Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa
    pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
48 Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?
    Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?
            Sela
49 Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,
    chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
50 Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,
    momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
51 mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,
    ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52 “Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”
Ameni ndi Ameni.

Psalm 89[a]

A maskil[b] of Ethan the Ezrahite.

I will sing(A) of the Lord’s great love forever;
    with my mouth I will make your faithfulness known(B)
    through all generations.
I will declare that your love stands firm forever,
    that you have established your faithfulness in heaven itself.(C)
You said, “I have made a covenant with my chosen one,
    I have sworn to David my servant,
‘I will establish your line forever
    and make your throne firm through all generations.’”[c](D)

The heavens(E) praise your wonders, Lord,
    your faithfulness too, in the assembly(F) of the holy ones.
For who in the skies above can compare with the Lord?
    Who is like the Lord among the heavenly beings?(G)
In the council(H) of the holy ones(I) God is greatly feared;
    he is more awesome than all who surround him.(J)
Who is like you,(K) Lord God Almighty?(L)
    You, Lord, are mighty, and your faithfulness surrounds you.

You rule over the surging sea;
    when its waves mount up, you still them.(M)
10 You crushed Rahab(N) like one of the slain;
    with your strong arm you scattered(O) your enemies.
11 The heavens are yours,(P) and yours also the earth;(Q)
    you founded the world and all that is in it.(R)
12 You created the north and the south;
    Tabor(S) and Hermon(T) sing for joy(U) at your name.
13 Your arm is endowed with power;
    your hand is strong, your right hand exalted.(V)

14 Righteousness and justice are the foundation of your throne;(W)
    love and faithfulness go before you.(X)
15 Blessed are those who have learned to acclaim you,
    who walk(Y) in the light(Z) of your presence, Lord.
16 They rejoice in your name(AA) all day long;
    they celebrate your righteousness.
17 For you are their glory and strength,(AB)
    and by your favor you exalt our horn.[d](AC)
18 Indeed, our shield[e](AD) belongs to the Lord,
    our king(AE) to the Holy One of Israel.

19 Once you spoke in a vision,
    to your faithful people you said:
“I have bestowed strength on a warrior;
    I have raised up a young man from among the people.
20 I have found David(AF) my servant;(AG)
    with my sacred oil(AH) I have anointed(AI) him.
21 My hand will sustain him;
    surely my arm will strengthen him.(AJ)
22 The enemy will not get the better of him;(AK)
    the wicked will not oppress(AL) him.
23 I will crush his foes before him(AM)
    and strike down his adversaries.(AN)
24 My faithful love will be with him,(AO)
    and through my name his horn[f] will be exalted.
25 I will set his hand over the sea,
    his right hand over the rivers.(AP)
26 He will call out to me, ‘You are my Father,(AQ)
    my God, the Rock(AR) my Savior.’(AS)
27 And I will appoint him to be my firstborn,(AT)
    the most exalted(AU) of the kings(AV) of the earth.
28 I will maintain my love to him forever,
    and my covenant with him will never fail.(AW)
29 I will establish his line forever,
    his throne as long as the heavens endure.(AX)

30 “If his sons forsake my law
    and do not follow my statutes,
31 if they violate my decrees
    and fail to keep my commands,
32 I will punish their sin with the rod,
    their iniquity with flogging;(AY)
33 but I will not take my love from him,(AZ)
    nor will I ever betray my faithfulness.
34 I will not violate my covenant
    or alter what my lips have uttered.(BA)
35 Once for all, I have sworn by my holiness—
    and I will not lie to David—
36 that his line will continue forever
    and his throne endure before me like the sun;(BB)
37 it will be established forever like the moon,
    the faithful witness in the sky.”(BC)

38 But you have rejected,(BD) you have spurned,
    you have been very angry with your anointed one.
39 You have renounced the covenant with your servant
    and have defiled his crown in the dust.(BE)
40 You have broken through all his walls(BF)
    and reduced his strongholds(BG) to ruins.
41 All who pass by have plundered(BH) him;
    he has become the scorn of his neighbors.(BI)
42 You have exalted the right hand of his foes;
    you have made all his enemies rejoice.(BJ)
43 Indeed, you have turned back the edge of his sword
    and have not supported him in battle.(BK)
44 You have put an end to his splendor
    and cast his throne to the ground.
45 You have cut short(BL) the days of his youth;
    you have covered him with a mantle of shame.(BM)

46 How long, Lord? Will you hide yourself forever?
    How long will your wrath burn like fire?(BN)
47 Remember how fleeting is my life.(BO)
    For what futility you have created all humanity!
48 Who can live and not see death,
    or who can escape the power of the grave?(BP)
49 Lord, where is your former great love,
    which in your faithfulness you swore to David?
50 Remember, Lord, how your servant has[g] been mocked,(BQ)
    how I bear in my heart the taunts of all the nations,
51 the taunts with which your enemies, Lord, have mocked,
    with which they have mocked every step of your anointed one.(BR)

52 Praise be to the Lord forever!
Amen and Amen.(BS)

Footnotes

  1. Psalm 89:1 In Hebrew texts 89:1-52 is numbered 89:2-53.
  2. Psalm 89:1 Title: Probably a literary or musical term
  3. Psalm 89:4 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 37, 45 and 48.
  4. Psalm 89:17 Horn here symbolizes strong one.
  5. Psalm 89:18 Or sovereign
  6. Psalm 89:24 Horn here symbolizes strength.
  7. Psalm 89:50 Or your servants have