Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide.

Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse;
    ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu;
    Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.

Adani anga amathawa,
    iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga;
    Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa;
    Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani,
    mwafafaniza mizinda yawo;
    ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.

Yehova akulamulira kwamuyaya;
    wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo;
    adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima,
    linga pa nthawi ya mavuto.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu,
    pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.

11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni;
    lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira;
    Iye salekerera kulira kwa ozunzika.

13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira!
    Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 kuti ndilengeze za matamando anu
    pa zipata za ana aakazi a Ziyoni,
    kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba;
    mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake;
    oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo.
            Higayoni. Sela
17 Oyipa amabwerera ku manda,
    mitundu yonse imene imayiwala Mulungu.
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse,
    kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.

19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane;
    mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova;
    mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba.
            Sela

Psalm 9[a][b]

For the director of music. To the tune of “The Death of the Son.” A psalm of David.

I will give thanks to you, Lord, with all my heart;(A)
    I will tell of all your wonderful deeds.(B)
I will be glad and rejoice(C) in you;
    I will sing the praises(D) of your name,(E) O Most High.

My enemies turn back;
    they stumble and perish before you.
For you have upheld my right(F) and my cause,(G)
    sitting enthroned(H) as the righteous judge.(I)
You have rebuked the nations(J) and destroyed the wicked;
    you have blotted out their name(K) for ever and ever.
Endless ruin has overtaken my enemies,
    you have uprooted their cities;(L)
    even the memory of them(M) has perished.

The Lord reigns forever;(N)
    he has established his throne(O) for judgment.
He rules the world in righteousness(P)
    and judges the peoples with equity.(Q)
The Lord is a refuge(R) for the oppressed,(S)
    a stronghold in times of trouble.(T)
10 Those who know your name(U) trust in you,
    for you, Lord, have never forsaken(V) those who seek you.(W)

11 Sing the praises(X) of the Lord, enthroned in Zion;(Y)
    proclaim among the nations(Z) what he has done.(AA)
12 For he who avenges blood(AB) remembers;
    he does not ignore the cries of the afflicted.(AC)

13 Lord, see how my enemies(AD) persecute me!
    Have mercy(AE) and lift me up from the gates of death,(AF)
14 that I may declare your praises(AG)
    in the gates of Daughter Zion,(AH)
    and there rejoice in your salvation.(AI)

15 The nations have fallen into the pit they have dug;(AJ)
    their feet are caught in the net they have hidden.(AK)
16 The Lord is known by his acts of justice;
    the wicked are ensnared by the work of their hands.[c](AL)
17 The wicked go down to the realm of the dead,(AM)
    all the nations that forget God.(AN)
18 But God will never forget the needy;
    the hope(AO) of the afflicted(AP) will never perish.

19 Arise,(AQ) Lord, do not let mortals triumph;(AR)
    let the nations be judged(AS) in your presence.
20 Strike them with terror,(AT) Lord;
    let the nations know they are only mortal.(AU)

Footnotes

  1. Psalm 9:1 Psalms 9 and 10 may originally have been a single acrostic poem in which alternating lines began with the successive letters of the Hebrew alphabet. In the Septuagint they constitute one psalm.
  2. Psalm 9:1 In Hebrew texts 9:1-20 is numbered 9:2-21.
  3. Psalm 9:16 The Hebrew has Higgaion and Selah (words of uncertain meaning) here; Selah occurs also at the end of verse 20.