Masalimo 91
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
91 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba
adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,
Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje
ndi ku mliri woopsa;
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake,
ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;
kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,
kapena muvi wowuluka masana,
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima,
kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,
anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,
koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
8 Udzapenya ndi maso ako
ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;
wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,
zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,
kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo,
kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka,
udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;
ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;
ndidzakhala naye pa mavuto,
ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali
ndi kumupulumutsa.”
Psalm 91
New International Version
Psalm 91
1 Whoever dwells in the shelter(A) of the Most High
will rest in the shadow(B) of the Almighty.[a]
2 I will say of the Lord, “He is my refuge(C) and my fortress,(D)
my God, in whom I trust.”
3 Surely he will save you
from the fowler’s snare(E)
and from the deadly pestilence.(F)
4 He will cover you with his feathers,
and under his wings you will find refuge;(G)
his faithfulness will be your shield(H) and rampart.
5 You will not fear(I) the terror of night,
nor the arrow that flies by day,
6 nor the pestilence that stalks in the darkness,
nor the plague that destroys at midday.
7 A thousand may fall at your side,
ten thousand at your right hand,
but it will not come near you.
8 You will only observe with your eyes
and see the punishment of the wicked.(J)
9 If you say, “The Lord is my refuge,”
and you make the Most High your dwelling,
10 no harm(K) will overtake you,
no disaster will come near your tent.
11 For he will command his angels(L) concerning you
to guard you in all your ways;(M)
12 they will lift you up in their hands,
so that you will not strike your foot against a stone.(N)
13 You will tread on the lion and the cobra;
you will trample the great lion and the serpent.(O)
Footnotes
- Psalm 91:1 Hebrew Shaddai
- Psalm 91:14 That is, probably the king
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.