Add parallel Print Page Options

97 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale;
    magombe akutali akondwere.

Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira;
    chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Moto umapita patsogolo pake
    ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse;
    dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova,
    pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake,
    ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.

Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi,
    iwo amene amanyadira mafano;
    mulambireni, inu milungu yonse!

Ziyoni akumva ndipo akukondwera,
    midzi ya Yuda ikusangalala
    chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi;
    ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.

10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa
    pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira
    ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama,
    ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama
    ndipo tamandani dzina lake loyera.

Psalm 97

The Lord reigns,(A) let the earth be glad;(B)
    let the distant shores(C) rejoice.
Clouds(D) and thick darkness(E) surround him;
    righteousness and justice are the foundation of his throne.(F)
Fire(G) goes before(H) him
    and consumes(I) his foes on every side.
His lightning(J) lights up the world;
    the earth(K) sees and trembles.(L)
The mountains melt(M) like wax(N) before the Lord,
    before the Lord of all the earth.(O)
The heavens proclaim his righteousness,(P)
    and all peoples see his glory.(Q)

All who worship images(R) are put to shame,(S)
    those who boast in idols(T)
    worship him,(U) all you gods!(V)

Zion hears and rejoices
    and the villages of Judah are glad(W)
    because of your judgments,(X) Lord.
For you, Lord, are the Most High(Y) over all the earth;(Z)
    you are exalted(AA) far above all gods.
10 Let those who love the Lord hate evil,(AB)
    for he guards(AC) the lives of his faithful ones(AD)
    and delivers(AE) them from the hand of the wicked.(AF)
11 Light shines[a](AG) on the righteous(AH)
    and joy on the upright in heart.(AI)
12 Rejoice in the Lord,(AJ) you who are righteous,
    and praise his holy name.(AK)

Footnotes

  1. Psalm 97:11 One Hebrew manuscript and ancient versions (see also 112:4); most Hebrew manuscripts Light is sown