Add parallel Print Page Options

99 Yehova akulamulira,
    mitundu ya anthu injenjemere;
Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,
    dziko lapansi ligwedezeke.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;
    Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,
    Iye ndi woyera.

Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo
    Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;
mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Kwezani Yehova Mulungu wathu
    ndipo mulambireni pa mapazi ake;
    Iye ndi woyera.

Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,
    Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;
iwo anayitana Yehova
    ndipo Iyeyo anawayankha.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;
    iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

Inu Yehova Mulungu wathu,
    munawayankha iwo;
Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,
    ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Kwezani Yehova Mulungu wathu
    ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,
    pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Psalm 99

The Lord reigns,(A)
    let the nations tremble;(B)
he sits enthroned(C) between the cherubim,(D)
    let the earth shake.
Great is the Lord(E) in Zion;(F)
    he is exalted(G) over all the nations.
Let them praise(H) your great and awesome name(I)
    he is holy.(J)

The King(K) is mighty, he loves justice(L)
    you have established equity;(M)
in Jacob you have done
    what is just and right.(N)
Exalt(O) the Lord our God
    and worship at his footstool;
    he is holy.

Moses(P) and Aaron(Q) were among his priests,
    Samuel(R) was among those who called on his name;
they called on the Lord
    and he answered(S) them.
He spoke to them from the pillar of cloud;(T)
    they kept his statutes and the decrees he gave them.

Lord our God,
    you answered them;
you were to Israel a forgiving God,(U)
    though you punished(V) their misdeeds.[a]
Exalt the Lord our God
    and worship at his holy mountain,
    for the Lord our God is holy.

Footnotes

  1. Psalm 99:8 Or God, / an avenger of the wrongs done to them