Add parallel Print Page Options

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

102 Yehova imvani pemphero langa;
    kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Musandibisire nkhope yanu
    pamene ndili pa msautso.
Munditcherere khutu;
    pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;
    mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;
    ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula
    ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,
    monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala
    ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;
    iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa
    ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu,
    popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;
    Ine ndikufota ngati udzu.

12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;
    kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni
    pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;
    nthawi yoyikika yafika.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;
    fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,
    mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni
    ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;
    sadzanyoza kupempha kwawo.

18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,
    kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,
    kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,
    kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni
    ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu
    adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;
    Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Choncho Ine ndinati:
    “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;
    zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi
    ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;
    zidzatha ngati chovala.
Mudzazisintha ngati chovala
    ndipo zidzatayidwa.
27 Koma Inu simusintha,
    ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;
    zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”