Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

11 Mwa Yehova ine ndimathawiramo.
    Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,
    “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;
    ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,
pobisala pawo kuti alase
    olungama mtima.
Tsono ngati maziko awonongeka,
    olungama angachite chiyani?”

Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;
    Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.
Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;
    maso ake amawayesa.
Yehova amayesa olungama,
    koma moyo wake umadana ndi oyipa,
    amene amakonda zachiwawa.
Iye adzakhuthulira pa oyipa
    makala amoto ndi sulufule woyaka;
    mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

Pakuti Yehova ndi wolungama,
    Iye amakonda chilungamo;
    ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.