Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.

12 Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;
    okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Aliyense amanamiza mʼbale wake;
    ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.

Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo
    ndi pakamwa paliponse podzikuza.
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;
    pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”

“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu
    ndi kubuwula kwa anthu osowa,
Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,
    “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro
    monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,
    oyengedwa kasanu nʼkawiri.

Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo
    mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse
    anthu akamayamikira zochita zawo.