Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

123 Ndikweza maso anga kwa Inu,
    kwa Inu amene mumakhala kumwamba.
Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,
    monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,
choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,
    mpaka atichitire chifundo.

Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,
    pakuti tapirira chitonzo chachikulu.
Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,
    chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.