Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

125 Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,
    limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu,
    momwemonso Yehova azungulira anthu ake
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala
    pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,
kuti anthu olungamawo
    angachite nawonso zoyipa.

Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,
    amene ndi olungama mtima
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,
    Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.