Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.

131 Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,
    maso anga siwonyada;
sinditengeteka mtima
    ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
Koma moyo wanga ndawutontholetsa
    ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,
    moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.

Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.