Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

141 Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.
    Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;
    kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

Yehova ikani mlonda pakamwa panga;
    londerani khomo la pa milomo yanga.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;
    kuchita ntchito zonyansa
pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;
    musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;
    andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.
    Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
    Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,
    ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,
    ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;
    ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,
    ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,
    mpaka ine nditadutsa mwamtendere.