Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

40 Mofatsa ndinadikira Yehova
    Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,
    mʼthope ndi mʼchithaphwi;
Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe
    ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,
    nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.
Ambiri adzaona,
    nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

Ndi wodala munthu
    amakhulupirira Yehova;
amene sayembekezera kwa odzikuza,
    kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Zambiri, Yehova Mulungu wanga,
    ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.
Zinthu zimene munazikonzera ife
    palibe amene angathe kukuwerengerani.
Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,
    zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,
    koma makutu anga mwawatsekula;
zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo
    Inu simunazipemphe.
Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.
    Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;
    lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;
    sinditseka milomo yanga
    monga mukudziwa Inu Yehova.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;
    ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.
Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu
    pa msonkhano waukulu.

11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova;
    chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;
    machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.
Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,
    ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13 Pulumutseni Yehova;
    Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga
    achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene amakhumba chiwonongeko changa
    abwezedwe mwamanyazi.
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”
    abwerere akuchita manyazi.
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu
    akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
    nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;
    Ambuye andiganizire.
Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;
    Inu Mulungu wanga, musachedwe.