Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

41 Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;
    Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;
    Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko
    ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
Yehova adzamuthandiza pamene akudwala
    ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;
    chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,
    “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Pamene wina abwera kudzandiona,
    amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;
    kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.

Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,
    iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
“Matenda owopsa amugwira;
    sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,
    iye amene amadya pamodzi ndi ine
    watukula chidendene chake kulimbana nane.

10 Koma Yehova mundichititre chifundo,
    dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,
    pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga
    ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.

13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli
    kuchokera muyaya mpaka muyaya.
            Ameni ndi Ameni.