Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
    onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
    mvetserani mawu a pakamwa panga.

Alendo akundithira nkhondo;
    anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
    anthu amene salabadira za Mulungu.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
    Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
    mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
    ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
    pakuti ndi labwino.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
    ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.