Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.

55 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
    musakufulatire kupempha kwanga,
    mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
    chifukwa cha mawu a adani anga,
    chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
    ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.

Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
    mantha a imfa andigwera.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
    mantha aakulu andithetsa nzeru.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
    Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
Ndikanathawira kutali
    ndi kukakhala mʼchipululu.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
    kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
    pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
    nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
    kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.

12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine
    ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
    ndikanakabisala.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
    bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
    pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.

15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
    alowe mʼmanda ali amoyo
    pakuti choyipa chili pakati pawo.

16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu,
    ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Madzulo, mmawa ndi masana
    ndimalira mowawidwa mtima,
    ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa
    pa nkhondo imene yafika kulimbana nane,
    ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya,
    adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga,
chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa
    ndipo saopa Mulungu.

20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake;
    iye akuphwanya pangano ake.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala
    komabe nkhondo ili mu mtima mwake;
mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta,
    komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.

22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova
    ndipo Iye adzakulimbitsani;
    Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa
    kulowa mʼdzenje lachiwonongeko;
anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo
    sadzakhala moyo theka la masiku awo,

koma ine ndimadalira Inu.