Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho.

70 Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;
    Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga
    achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene akukhumba chiwonongeko changa
    abwezedwe mopanda ulemu.
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”
    abwerere chifukwa cha manyazi awo.
Koma onse amene akufunafuna Inu
    akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
    nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”

Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;
    bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;
    Inu Yehova musachedwe.