Add parallel Print Page Options

Salimo la Asafu.

82 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
    Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
    ndi kukondera anthu oyipa?
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
    mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
    apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
    Amayendayenda mu mdima;
    maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
    nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Koma mudzafa ngati anthu wamba;
    mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
    pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.