Add parallel Print Page Options

Salimo la Ana a Kora.

87 Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
    Yehova amakonda zipata za Ziyoni
    kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Za ulemerero wako zimakambidwa,
    Iwe mzinda wa Mulungu:
            Sela
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
    pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
    ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
    “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
    ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
    “Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
            Sela
Oyimba ndi ovina omwe adzati,
    “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”