Add parallel Print Page Options

Anzeru a Kummawa

Atabadwa Yesu mʼBetelehemu wa ku Yudeya, mʼnthawi ya mfumu Herode, Anzeru a kummawa anabwera ku Yerusalemu nafunsa kuti, “Ali kuti amene wabadwa kukhala mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kummawa ndipo tabwera kudzamupembedza.”

Mfumu Herode atamva zimenezi, anavutika mu mtima kwambiri pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu. Ndipo anayitanitsa anthu onse, akulu ansembe ndi aphunzitsi amalamulo nawafunsa kuti, “Kodi Khristu adzabadwira kuti?” Ndipo anamuyankha kuti, “Ku Betelehemu wa ku Yudeya chifukwa izi ndi zimene mneneri analemba kuti,

“ ‘Koma iwe Betelehemu, chigawo cha Yudeya,
    sindiwe wamngʼonongʼono mwa olamulira a Yudeya;
pakuti otsogolera adzachokera mwa iwe,
    amene adzaweta anthu anga Aisraeli.’ ”

Pomwepo Herode anawayitanira mseri Anzeruwo nawafunsitsa nthawi yeniyeni yomwe nyenyeziyo inaoneka. Ndipo anawatumiza ku Betelehemu nawawuza kuti, “Pitani mukafufuze za mwanayo mosamalitsa. Ndipo mukamupeza mudzandiwuze kuti inenso ndikamupembedze.”

Atamva mawu a mfumu, ananyamuka ulendo wawo, ndipo taonani nyenyezi anayiona kummawa ija, inawatsogolera mpaka inayima pamwamba pa nyumba yomwe munali mwanayo. 10 Pamene iwo anaona nyenyeziyo, anasangalala kwambiri. 11 Pofika ku nyumbayo, anaona mwanayo pamodzi ndi amayi ake Mariya, ndipo anagwada namulambira Iye. Pomwepo anamasula chuma chawo ndi kupereka mphatso zawo za ndalama zagolide, lubani ndi mure. 12 Ndipo atachenjezedwa mʼmaloto kuti asapitenso kwa Herode, anabwerera ku dziko la kwawo podzera njira ina.

Athawira ku Igupto

13 Atachoka, taonani mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto nati, “Tadzuka, tenga mwanayo pamodzi ndi amayi ake ndipo muthawire ku Igupto. Mukakhale kumeneko mpaka nditakuwuza pakuti Herode adzafunafuna mwanayo kuti amuphe.” 14 Atadzuka, Yosefe anatenga mwanayo ndi amayi ake usiku omwewo napita ku Igupto, 15 nakhala kumeneko mpaka Herode atamwalira. Ndipo zinakwaniritsidwa zomwe ananena Ambuye mwa mneneri kuti, “Ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.”

Kuphedwa kwa Ana mʼBetelehemu

16 Herode atazindikira kuti Anzeruwo anamupusitsa, anakwiya kwambiri. Ndipo anatumiza anthu kukapha ana onse aamuna a mʼBetelehemu ndi midzi yozungulira amene anali a zaka ziwiri kapena zocheperapo, molingana ndi nthawi imene Anzeruwo anamuwuza. 17 Pamenepo, zimene ananena mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa:

18 “Kulira kukumveka ku Rama,
    kubuma ndi kulira kwakukulu,
Rakele akulirira ana ake;
    sakutonthozeka,
chifukwa ana akewo palibe.”

Abwerera ku Nazareti

19 Atamwalira Herode, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto ku Igupto 20 nanena kuti, “Nyamuka, tenga mwanayo ndi amayi ake ndipo mupite ku dziko la Israeli, popeza amene anafuna moyo wa mwanayo anamwalira.”

21 Tsono Yosefe atadzuka anatenga mwanayo ndi amayi ake kupita ku dziko la Israeli. 22 Koma atamva kuti Arikelao akulamulira mu Yudeya mʼmalo mwa abambo ake, Herode, anaopa kupitako. Atachenjezedwa mʼmaloto, anapita ku Galileya, 23 ndipo anakakhazikika mu mzinda wa Nazareti. Pamenepo zinakwaniritsidwa zonenedwa ndi aneneri kuti, “Adzatchedwa Mnazareti.”

The Magi Visit the Messiah

After Jesus was born in Bethlehem in Judea,(A) during the time of King Herod,(B) Magi[a] from the east came to Jerusalem and asked, “Where is the one who has been born king of the Jews?(C) We saw his star(D) when it rose and have come to worship him.”

When King Herod heard this he was disturbed, and all Jerusalem with him. When he had called together all the people’s chief priests and teachers of the law, he asked them where the Messiah was to be born. “In Bethlehem(E) in Judea,” they replied, “for this is what the prophet has written:

“‘But you, Bethlehem, in the land of Judah,
    are by no means least among the rulers of Judah;
for out of you will come a ruler
    who will shepherd my people Israel.’[b](F)

Then Herod called the Magi secretly and found out from them the exact time the star had appeared. He sent them to Bethlehem and said, “Go and search carefully for the child. As soon as you find him, report to me, so that I too may go and worship him.”

After they had heard the king, they went on their way, and the star they had seen when it rose went ahead of them until it stopped over the place where the child was. 10 When they saw the star, they were overjoyed. 11 On coming to the house, they saw the child with his mother Mary, and they bowed down and worshiped him.(G) Then they opened their treasures and presented him with gifts(H) of gold, frankincense and myrrh. 12 And having been warned(I) in a dream(J) not to go back to Herod, they returned to their country by another route.

The Escape to Egypt

13 When they had gone, an angel(K) of the Lord appeared to Joseph in a dream.(L) “Get up,” he said, “take the child and his mother and escape to Egypt. Stay there until I tell you, for Herod is going to search for the child to kill him.”(M)

14 So he got up, took the child and his mother during the night and left for Egypt, 15 where he stayed until the death of Herod. And so was fulfilled(N) what the Lord had said through the prophet: “Out of Egypt I called my son.”[c](O)

16 When Herod realized that he had been outwitted by the Magi, he was furious, and he gave orders to kill all the boys in Bethlehem and its vicinity who were two years old and under, in accordance with the time he had learned from the Magi. 17 Then what was said through the prophet Jeremiah was fulfilled:(P)

18 “A voice is heard in Ramah,
    weeping and great mourning,
Rachel(Q) weeping for her children
    and refusing to be comforted,
    because they are no more.”[d](R)

The Return to Nazareth

19 After Herod died, an angel(S) of the Lord appeared in a dream(T) to Joseph in Egypt 20 and said, “Get up, take the child and his mother and go to the land of Israel, for those who were trying to take the child’s life are dead.”(U)

21 So he got up, took the child and his mother and went to the land of Israel. 22 But when he heard that Archelaus was reigning in Judea in place of his father Herod, he was afraid to go there. Having been warned in a dream,(V) he withdrew to the district of Galilee,(W) 23 and he went and lived in a town called Nazareth.(X) So was fulfilled(Y) what was said through the prophets, that he would be called a Nazarene.(Z)

Footnotes

  1. Matthew 2:1 Traditionally wise men
  2. Matthew 2:6 Micah 5:2,4
  3. Matthew 2:15 Hosea 11:1
  4. Matthew 2:18 Jer. 31:15