Add parallel Print Page Options

Zizindikiro za Masiku Otsiriza

24 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”

Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?”

Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri. Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike. Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana. Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.

“Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine. 10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake, 11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri. 12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala, 13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka. 14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”

15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire. 16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri. 17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba. 18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake. 19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa! 20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata. 21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena. 22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa. 23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire. 24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero. 25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.

26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire. 27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu. 28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.

29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo,

“ ‘dzuwa lidzadetsedwa,
    ndipo mwezi sudzawala;
nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba,
    ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’

30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu. 31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.

32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira. 33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni. 34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika. 35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Tsiku ndi Nthawi Sizidziwika

36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha. 37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu. 38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo; 39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu. 40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala. 41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.

42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera. 43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe. 44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.

Wantchito Wokhulupirika ndi Wosakhulupirika

45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani? 46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi. 47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense. 48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’ 49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa. 50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa. 51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”

The Destruction of the Temple and Signs of the End Times(A)

24 Jesus left the temple and was walking away when his disciples came up to him to call his attention to its buildings. “Do you see all these things?” he asked. “Truly I tell you, not one stone here will be left on another;(B) every one will be thrown down.”

As Jesus was sitting on the Mount of Olives,(C) the disciples came to him privately. “Tell us,” they said, “when will this happen, and what will be the sign of your coming(D) and of the end of the age?”(E)

Jesus answered: “Watch out that no one deceives you.(F) For many will come in my name, claiming, ‘I am the Messiah,’ and will deceive many.(G) You will hear of wars and rumors of wars, but see to it that you are not alarmed. Such things must happen, but the end is still to come. Nation will rise against nation, and kingdom against kingdom.(H) There will be famines(I) and earthquakes in various places. All these are the beginning of birth pains.

“Then you will be handed over to be persecuted(J) and put to death,(K) and you will be hated by all nations because of me.(L) 10 At that time many will turn away from the faith and will betray and hate each other, 11 and many false prophets(M) will appear and deceive many people.(N) 12 Because of the increase of wickedness, the love of most will grow cold, 13 but the one who stands firm to the end will be saved.(O) 14 And this gospel of the kingdom(P) will be preached in the whole world(Q) as a testimony to all nations, and then the end will come.

15 “So when you see standing in the holy place(R) ‘the abomination that causes desolation,’[a](S) spoken of through the prophet Daniel—let the reader understand— 16 then let those who are in Judea flee to the mountains. 17 Let no one on the housetop(T) go down to take anything out of the house. 18 Let no one in the field go back to get their cloak. 19 How dreadful it will be in those days for pregnant women and nursing mothers!(U) 20 Pray that your flight will not take place in winter or on the Sabbath. 21 For then there will be great distress, unequaled from the beginning of the world until now—and never to be equaled again.(V)

22 “If those days had not been cut short, no one would survive, but for the sake of the elect(W) those days will be shortened. 23 At that time if anyone says to you, ‘Look, here is the Messiah!’ or, ‘There he is!’ do not believe it.(X) 24 For false messiahs and false prophets will appear and perform great signs and wonders(Y) to deceive, if possible, even the elect. 25 See, I have told you ahead of time.

26 “So if anyone tells you, ‘There he is, out in the wilderness,’ do not go out; or, ‘Here he is, in the inner rooms,’ do not believe it. 27 For as lightning(Z) that comes from the east is visible even in the west, so will be the coming(AA) of the Son of Man.(AB) 28 Wherever there is a carcass, there the vultures will gather.(AC)

29 “Immediately after the distress of those days

“‘the sun will be darkened,
    and the moon will not give its light;
the stars will fall from the sky,
    and the heavenly bodies will be shaken.’[b](AD)

30 “Then will appear the sign of the Son of Man in heaven. And then all the peoples of the earth[c] will mourn(AE) when they see the Son of Man coming on the clouds of heaven,(AF) with power and great glory.[d] 31 And he will send his angels(AG) with a loud trumpet call,(AH) and they will gather his elect from the four winds, from one end of the heavens to the other.

32 “Now learn this lesson from the fig tree: As soon as its twigs get tender and its leaves come out, you know that summer is near. 33 Even so, when you see all these things, you know that it[e] is near, right at the door.(AI) 34 Truly I tell you, this generation will certainly not pass away until all these things have happened.(AJ) 35 Heaven and earth will pass away, but my words will never pass away.(AK)

The Day and Hour Unknown(AL)(AM)

36 “But about that day or hour no one knows, not even the angels in heaven, nor the Son,[f] but only the Father.(AN) 37 As it was in the days of Noah,(AO) so it will be at the coming of the Son of Man. 38 For in the days before the flood, people were eating and drinking, marrying and giving in marriage,(AP) up to the day Noah entered the ark; 39 and they knew nothing about what would happen until the flood came and took them all away. That is how it will be at the coming of the Son of Man.(AQ) 40 Two men will be in the field; one will be taken and the other left.(AR) 41 Two women will be grinding with a hand mill; one will be taken and the other left.(AS)

42 “Therefore keep watch, because you do not know on what day your Lord will come.(AT) 43 But understand this: If the owner of the house had known at what time of night the thief was coming,(AU) he would have kept watch and would not have let his house be broken into. 44 So you also must be ready,(AV) because the Son of Man will come at an hour when you do not expect him.

45 “Who then is the faithful and wise servant,(AW) whom the master has put in charge of the servants in his household to give them their food at the proper time? 46 It will be good for that servant whose master finds him doing so when he returns.(AX) 47 Truly I tell you, he will put him in charge of all his possessions.(AY) 48 But suppose that servant is wicked and says to himself, ‘My master is staying away a long time,’ 49 and he then begins to beat his fellow servants and to eat and drink with drunkards.(AZ) 50 The master of that servant will come on a day when he does not expect him and at an hour he is not aware of. 51 He will cut him to pieces and assign him a place with the hypocrites, where there will be weeping and gnashing of teeth.(BA)

Footnotes

  1. Matthew 24:15 Daniel 9:27; 11:31; 12:11
  2. Matthew 24:29 Isaiah 13:10; 34:4
  3. Matthew 24:30 Or the tribes of the land
  4. Matthew 24:30 See Daniel 7:13-14.
  5. Matthew 24:33 Or he
  6. Matthew 24:36 Some manuscripts do not have nor the Son.