Add parallel Print Page Options

Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,
    mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,
pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,
    Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;
    Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
Mapiri akusungunuka pansi pake,
    ndipo zigwa zikugawikana
ngati phula pa moto,
    ngati madzi ochokera mʼphiri.
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,
    chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.
Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?
    Kodi si Samariya?
Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?
    Kodi si Yerusalemu?

“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,
    malo odzalamo mphesa.
Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa
    ndipo ndidzafukula maziko ake.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;
    mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;
    ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.
Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,
    mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;
    ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.
Ndidzafuwula ngati nkhandwe
    ndi kulira ngati kadzidzi.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;
    chafika ku Yuda.
Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,
    mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Musanene zimenezi ku Gati;
    musalire nʼkomwe.
Mugubuduzike mu fumbi
    ku Beti-Leafura.
11 Inu anthu okhala ku Safiro,
    muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.
Iwo amene akukhala ku Zanaani
    sadzatuluka.
Beti-Ezeli akulira mwachisoni;
    chitetezo chake chakuchokerani.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,
    akuyembekezera thandizo,
chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,
    lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi
    mangani akavalo ku magaleta.
Inu amene munayamba kuchimwitsa
    mwana wamkazi wa Ziyoni,
pakuti zolakwa za Israeli
    zinapezeka pakati panu.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana
    ndi a ku Moreseti Gati.
Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama
    kwa mafumu a Israeli.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu
    okhala mu Maresa.
Ulemerero wa Israeli udzafika
    ku Adulamu.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira
    ana anu amene mumawakonda;
mudzichititse dazi ngati dembo,
    pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

The word of the Lord that came to Micah of Moresheth(A) during the reigns of Jotham,(B) Ahaz(C) and Hezekiah,(D) kings of Judah(E)—the vision(F) he saw concerning Samaria and Jerusalem.

Hear,(G) you peoples, all of you,(H)
    listen, earth(I) and all who live in it,
that the Sovereign Lord may bear witness(J) against you,
    the Lord from his holy temple.(K)

Judgment Against Samaria and Jerusalem

Look! The Lord is coming from his dwelling(L) place;
    he comes down(M) and treads on the heights of the earth.(N)
The mountains melt(O) beneath him(P)
    and the valleys split apart,(Q)
like wax before the fire,
    like water rushing down a slope.
All this is because of Jacob’s transgression,
    because of the sins of the people of Israel.
What is Jacob’s transgression?
    Is it not Samaria?(R)
What is Judah’s high place?
    Is it not Jerusalem?

“Therefore I will make Samaria a heap of rubble,
    a place for planting vineyards.(S)
I will pour her stones(T) into the valley
    and lay bare her foundations.(U)
All her idols(V) will be broken to pieces;(W)
    all her temple gifts will be burned with fire;
    I will destroy all her images.(X)
Since she gathered her gifts from the wages of prostitutes,(Y)
    as the wages of prostitutes they will again be used.”

Weeping and Mourning

Because of this I will weep(Z) and wail;
    I will go about barefoot(AA) and naked.
I will howl like a jackal
    and moan like an owl.
For Samaria’s plague(AB) is incurable;(AC)
    it has spread to Judah.(AD)
It has reached the very gate(AE) of my people,
    even to Jerusalem itself.
10 Tell it not in Gath[a];
    weep not at all.
In Beth Ophrah[b]
    roll in the dust.
11 Pass by naked(AF) and in shame,
    you who live in Shaphir.[c]
Those who live in Zaanan[d]
    will not come out.
Beth Ezel is in mourning;
    it no longer protects you.
12 Those who live in Maroth[e] writhe in pain,
    waiting for relief,(AG)
because disaster(AH) has come from the Lord,
    even to the gate of Jerusalem.
13 You who live in Lachish,(AI)
    harness fast horses to the chariot.
You are where the sin of Daughter Zion(AJ) began,
    for the transgressions of Israel were found in you.
14 Therefore you will give parting gifts(AK)
    to Moresheth(AL) Gath.
The town of Akzib[f](AM) will prove deceptive(AN)
    to the kings of Israel.
15 I will bring a conqueror against you
    who live in Mareshah.[g](AO)
The nobles of Israel
    will flee to Adullam.(AP)
16 Shave(AQ) your head in mourning
    for the children in whom you delight;
make yourself as bald as the vulture,
    for they will go from you into exile.(AR)

Footnotes

  1. Micah 1:10 Gath sounds like the Hebrew for tell.
  2. Micah 1:10 Beth Ophrah means house of dust.
  3. Micah 1:11 Shaphir means pleasant.
  4. Micah 1:11 Zaanan sounds like the Hebrew for come out.
  5. Micah 1:12 Maroth sounds like the Hebrew for bitter.
  6. Micah 1:14 Akzib means deception.
  7. Micah 1:15 Mareshah sounds like the Hebrew for conqueror.