Add parallel Print Page Options

Zokonzekera za Munthu ndi Zokonzekera za Mulungu

Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu,
    kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo!
Kukacha mmawa amakachitadi
    chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Amasirira minda ndi kuyilanda,
    amasirira nyumba ndi kuzilanda.
Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo,
    munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.

Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa,
    tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha.
Inu simudzayendanso monyada,
    pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe;
    adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro:
‘Tawonongeka kotheratu;
    dziko la anthu anga lagawidwa.
Iye wandilanda!
    Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’ ”

Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova
    kuti agawe dziko pochita maere.

Aneneri Onyenga

Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere!
    Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi;
    ife sitidzachititsidwa manyazi.”
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena:
    “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya?
    Kodi Iye amachita zinthu zotere?”

“Kodi mawu ake sabweretsa zabwino
    kwa amene amayenda molungama?
Posachedwapa anthu anga andiwukira
    ngati mdani.
Mumawavula mkanjo wamtengowapatali
    anthu amene amadutsa mosaopa kanthu,
    monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
Mumatulutsa akazi a anthu anga
    mʼnyumba zawo zabwino.
Mumalanda ana awo madalitso anga
    kosatha.
10 Nyamukani, chokani!
    Pakuti ano si malo anu opumulirapo,
chifukwa ayipitsidwa,
    awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti,
    ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri,
    woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’

Alonjeza Chipulumutso

12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse;
    ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli.
Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola,
    ngati ziweto pa msipu wake;
    malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo;
    iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka.
Mfumu yawo idzawatsogolera,
    Yehova adzakhala patsogolo pawo.”

Human Plans and God’s Plans

Woe to those who plan iniquity,
    to those who plot evil(A) on their beds!(B)
At morning’s light they carry it out
    because it is in their power to do it.
They covet fields(C) and seize them,(D)
    and houses, and take them.
They defraud(E) people of their homes,
    they rob them of their inheritance.(F)

Therefore, the Lord says:

“I am planning disaster(G) against this people,
    from which you cannot save yourselves.
You will no longer walk proudly,(H)
    for it will be a time of calamity.
In that day people will ridicule you;
    they will taunt you with this mournful song:
‘We are utterly ruined;(I)
    my people’s possession is divided up.(J)
He takes it from me!
    He assigns our fields to traitors.’”

Therefore you will have no one in the assembly of the Lord
    to divide the land(K) by lot.(L)

False Prophets

“Do not prophesy,” their prophets say.
    “Do not prophesy about these things;
    disgrace(M) will not overtake us.(N)
You descendants of Jacob, should it be said,
    “Does the Lord become[a] impatient?
    Does he do such things?”

“Do not my words do good(O)
    to the one whose ways are upright?(P)
Lately my people have risen up
    like an enemy.
You strip off the rich robe
    from those who pass by without a care,
    like men returning from battle.
You drive the women of my people
    from their pleasant homes.(Q)
You take away my blessing
    from their children forever.
10 Get up, go away!
    For this is not your resting place,(R)
because it is defiled,(S)
    it is ruined, beyond all remedy.
11 If a liar and deceiver(T) comes and says,
    ‘I will prophesy for you plenty of wine and beer,’(U)
    that would be just the prophet for this people!(V)

Deliverance Promised

12 “I will surely gather all of you, Jacob;
    I will surely bring together the remnant(W) of Israel.
I will bring them together like sheep in a pen,
    like a flock in its pasture;
    the place will throng with people.(X)
13 The One who breaks open the way will go up before(Y) them;
    they will break through the gate(Z) and go out.
Their King will pass through before them,
    the Lord at their head.”

Footnotes

  1. Micah 2:7 Or Is the Spirit of the Lord