Add parallel Print Page Options

Phiri la Yehova

Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
    kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.
Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
    ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.

Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,
    ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
    ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
    mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri
    ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
    ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
    kapena kuphunziranso za nkhondo.
Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa
    ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,
ndipo palibe amene adzawachititse mantha,
    pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
Mitundu yonse ya anthu
    itha kutsatira milungu yawo;
ife tidzayenda mʼnjira za Yehova
    Mulungu wathu mpaka muyaya.

Cholinga cha Yehova

“Tsiku limenelo, Yehova akuti,

“ndidzasonkhanitsa olumala;
    ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa
    ndiponso amene ndinawalanga.
Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.
    Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.
Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova
    kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,
    iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,
ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;
    ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”

Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,
    kodi ulibe mfumu?
Kodi phungu wako wawonongedwa,
    kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,
    ngati mayi pa nthawi yake yobereka,
pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda
    ndi kugona kunja kwa mzindawo.
Udzapita ku Babuloni;
    kumeneko udzapulumutsidwa,
kumeneko Yehova adzakuwombola
    mʼmanja mwa adani ako.

11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu
    yasonkhana kulimbana nawe.
Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,
    maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
12 Koma iwo sakudziwa
    maganizo a Yehova;
iwo sakuzindikira cholinga chake,
    Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.

13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,
    pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;
ndidzakupatsa ziboda zamkuwa
    ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”

Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,
    chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.

The Mountain of the Lord(A)

In the last days

the mountain(B) of the Lord’s temple will be established
    as the highest of the mountains;
it will be exalted above the hills,(C)
    and peoples will stream to it.(D)

Many nations will come and say,

“Come, let us go up to the mountain of the Lord,(E)
    to the temple of the God of Jacob.(F)
He will teach us(G) his ways,(H)
    so that we may walk in his paths.”
The law(I) will go out from Zion,
    the word of the Lord from Jerusalem.
He will judge between many peoples
    and will settle disputes for strong nations far and wide.(J)
They will beat their swords into plowshares
    and their spears into pruning hooks.(K)
Nation will not take up sword against nation,
    nor will they train for war(L) anymore.(M)
Everyone will sit under their own vine
    and under their own fig tree,(N)
and no one will make them afraid,(O)
    for the Lord Almighty has spoken.(P)
All the nations may walk
    in the name of their gods,(Q)
but we will walk in the name of the Lord
    our God for ever and ever.(R)

The Lord’s Plan

“In that day,” declares the Lord,

“I will gather the lame;(S)
    I will assemble the exiles(T)
    and those I have brought to grief.(U)
I will make the lame my remnant,(V)
    those driven away a strong nation.(W)
The Lord will rule over them in Mount Zion(X)
    from that day and forever.(Y)
As for you, watchtower of the flock,
    stronghold[a] of Daughter Zion,
the former dominion will be restored(Z) to you;
    kingship will come to Daughter Jerusalem.(AA)

Why do you now cry aloud—
    have you no king[b](AB)?
Has your ruler[c] perished,
    that pain seizes you like that of a woman in labor?(AC)
10 Writhe in agony, Daughter Zion,
    like a woman in labor,
for now you must leave the city
    to camp in the open field.
You will go to Babylon;(AD)
    there you will be rescued.
There the Lord will redeem(AE) you
    out of the hand of your enemies.

11 But now many nations
    are gathered against you.
They say, “Let her be defiled,
    let our eyes gloat(AF) over Zion!”
12 But they do not know
    the thoughts of the Lord;
they do not understand his plan,(AG)
    that he has gathered them like sheaves to the threshing floor.
13 “Rise and thresh,(AH) Daughter Zion,
    for I will give you horns of iron;
I will give you hooves of bronze,
    and you will break to pieces many nations.”(AI)
You will devote their ill-gotten gains to the Lord,(AJ)
    their wealth to the Lord of all the earth.

Footnotes

  1. Micah 4:8 Or hill
  2. Micah 4:9 Or King
  3. Micah 4:9 Or Ruler