Add parallel Print Page Options

12 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu,
    koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.

Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova,
    koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.

Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa,
    koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.

Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake,
    koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.

Maganizo a anthu olungama ndi owongoka,
    koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.

Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa,
    koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.

Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika,
    koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.

Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake,
    koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.

Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika,
    kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.

10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake,
    koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.

11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka,
    koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.

12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa,
    koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.

13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa;
    koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.

14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake
    ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.

15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino,
    koma munthu wanzeru amamvera malangizo.

16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo,
    koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.

17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona,
    koma mboni yabodza imafotokoza zonama.

18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga,
    koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.

19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya
    koma mawu abodza sakhalitsa.

20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo;
    koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.

21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama,
    koma munthu woyipa mavuto samuthera.

22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova,
    koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.

23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake,
    koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.

24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira,
    koma aulesi adzakhala ngati kapolo.

25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu,
    koma mawu abwino amamusangalatsa.

26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake,
    koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.

27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna,
    koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.

28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo;
    koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

12 Whoever loves discipline loves knowledge,
    but whoever hates correction is stupid.(A)

Good people obtain favor from the Lord,(B)
    but he condemns those who devise wicked schemes.(C)

No one can be established through wickedness,
    but the righteous cannot be uprooted.(D)

A wife of noble character(E) is her husband’s crown,
    but a disgraceful wife is like decay in his bones.(F)

The plans of the righteous are just,
    but the advice of the wicked is deceitful.

The words of the wicked lie in wait for blood,
    but the speech of the upright rescues them.(G)

The wicked are overthrown and are no more,(H)
    but the house of the righteous stands firm.(I)

A person is praised according to their prudence,
    and one with a warped(J) mind is despised.

Better to be a nobody and yet have a servant
    than pretend to be somebody and have no food.

10 The righteous care for the needs of their animals,(K)
    but the kindest acts of the wicked are cruel.

11 Those who work their land will have abundant food,
    but those who chase fantasies have no sense.(L)

12 The wicked desire the stronghold of evildoers,
    but the root of the righteous endures.

13 Evildoers are trapped by their sinful talk,(M)
    and so the innocent escape trouble.(N)

14 From the fruit of their lips people are filled with good things,(O)
    and the work of their hands brings them reward.(P)

15 The way of fools seems right to them,(Q)
    but the wise listen to advice.(R)

16 Fools(S) show their annoyance at once,(T)
    but the prudent overlook an insult.(U)

17 An honest witness tells the truth,
    but a false witness tells lies.(V)

18 The words of the reckless pierce like swords,(W)
    but the tongue of the wise brings healing.(X)

19 Truthful lips endure forever,
    but a lying tongue lasts only a moment.

20 Deceit is in the hearts of those who plot evil,
    but those who promote peace have joy.(Y)

21 No harm overtakes the righteous,(Z)
    but the wicked have their fill of trouble.

22 The Lord detests lying lips,(AA)
    but he delights(AB) in people who are trustworthy.(AC)

23 The prudent keep their knowledge to themselves,(AD)
    but a fool’s heart blurts out folly.(AE)

24 Diligent hands will rule,
    but laziness ends in forced labor.(AF)

25 Anxiety weighs down the heart,(AG)
    but a kind word cheers it up.

26 The righteous choose their friends carefully,
    but the way of the wicked leads them astray.(AH)

27 The lazy do not roast[a] any game,
    but the diligent feed on the riches of the hunt.

28 In the way of righteousness there is life;(AI)
    along that path is immortality.

Footnotes

  1. Proverbs 12:27 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.