Add parallel Print Page Options

15 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,
    koma mawu ozaza amautsa ukali.

Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,
    koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.

Maso a Yehova ali ponseponse,
    amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.

Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,
    koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.

Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,
    koma wochenjera amasamala chidzudzulo.

Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,
    zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.

Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;
    koma mitima ya zitsiru sitero.

Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,
    koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.

Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova
    koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.

10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.
    Odana ndi chidzudzulo adzafa.

11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,
    nanji mitima ya anthu!

12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;
    iye sapita kwa anthu anzeru.

13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,
    koma mtima wosweka umawawitsa moyo.

14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,
    koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.

15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,
    koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.

16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,
    kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.

17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,
    kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.

18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano,
    koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.

19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga,
    koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.

20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,
    koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.

21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru,
    koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.

22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,
    koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.

23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,
    ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.

24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo
    kuti apewe malo okhala anthu akufa.

25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada
    koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.

26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova,
    koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.

27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake,
    koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.

28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire,
    koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.

29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa,
    koma amamva pemphero la anthu olungama.

30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima
    ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.

31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo
    adzakhala pakati pa anthu anzeru.

32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha,
    koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.

33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru,
    ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

15 A gentle answer(A) turns away wrath,(B)
    but a harsh word stirs up anger.

The tongue of the wise adorns knowledge,(C)
    but the mouth of the fool gushes folly.(D)

The eyes(E) of the Lord are everywhere,(F)
    keeping watch on the wicked and the good.(G)

The soothing tongue(H) is a tree of life,(I)
    but a perverse tongue crushes the spirit.(J)

A fool spurns a parent’s discipline,
    but whoever heeds correction shows prudence.(K)

The house of the righteous contains great treasure,(L)
    but the income of the wicked brings ruin.(M)

The lips of the wise spread knowledge,(N)
    but the hearts of fools are not upright.

The Lord detests the sacrifice(O) of the wicked,(P)
    but the prayer of the upright pleases him.(Q)

The Lord detests the way of the wicked,(R)
    but he loves those who pursue righteousness.(S)

10 Stern discipline awaits anyone who leaves the path;
    the one who hates correction will die.(T)

11 Death and Destruction[a] lie open before the Lord(U)
    how much more do human hearts!(V)

12 Mockers resent correction,(W)
    so they avoid the wise.

13 A happy heart makes the face cheerful,(X)
    but heartache crushes the spirit.(Y)

14 The discerning heart seeks knowledge,(Z)
    but the mouth of a fool feeds on folly.

15 All the days of the oppressed are wretched,
    but the cheerful heart has a continual feast.(AA)

16 Better a little with the fear of the Lord
    than great wealth with turmoil.(AB)

17 Better a small serving of vegetables with love
    than a fattened calf with hatred.(AC)

18 A hot-tempered person stirs up conflict,(AD)
    but the one who is patient calms a quarrel.(AE)

19 The way of the sluggard is blocked with thorns,(AF)
    but the path of the upright is a highway.

20 A wise son brings joy to his father,(AG)
    but a foolish man despises his mother.

21 Folly brings joy to one who has no sense,(AH)
    but whoever has understanding keeps a straight course.

22 Plans fail for lack of counsel,(AI)
    but with many advisers(AJ) they succeed.(AK)

23 A person finds joy in giving an apt reply(AL)
    and how good is a timely word!(AM)

24 The path of life leads upward for the prudent
    to keep them from going down to the realm of the dead.

25 The Lord tears down the house of the proud,(AN)
    but he sets the widow’s boundary stones in place.(AO)

26 The Lord detests the thoughts(AP) of the wicked,(AQ)
    but gracious words are pure(AR) in his sight.

27 The greedy bring ruin to their households,
    but the one who hates bribes will live.(AS)

28 The heart of the righteous weighs its answers,(AT)
    but the mouth of the wicked gushes evil.(AU)

29 The Lord is far from the wicked,
    but he hears the prayer of the righteous.(AV)

30 Light in a messenger’s eyes brings joy to the heart,
    and good news gives health to the bones.(AW)

31 Whoever heeds life-giving correction
    will be at home among the wise.(AX)

32 Those who disregard discipline despise themselves,(AY)
    but the one who heeds correction gains understanding.(AZ)

33 Wisdom’s instruction is to fear the Lord,(BA)
    and humility comes before honor.(BB)

Footnotes

  1. Proverbs 15:11 Hebrew Abaddon