Add parallel Print Page Options

16 Zolinga za mu mtima ndi za munthu,
    koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,
    koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,
    ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,
    ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.
    Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;
    chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,
    ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,
    kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

Mtima wa munthu umalingalira zochita,
    koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;
    ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;
    miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,
    pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13 Mawu owona amakondweretsa mfumu.
    Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,
    koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;
    ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.
    Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;
    wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,
    ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,
    kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,
    ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,
    ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,
    koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,
    ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,
    amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu
    koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;
    njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa
    ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,
    ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake,
    ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;
    amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;
    munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,
    munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33 Maere amaponyedwa pa mfunga,
    koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

16 To humans belong the plans of the heart,
    but from the Lord comes the proper answer of the tongue.(A)

All a person’s ways seem pure to them,(B)
    but motives are weighed(C) by the Lord.(D)

Commit to the Lord whatever you do,
    and he will establish your plans.(E)

The Lord works out everything to its proper end(F)
    even the wicked for a day of disaster.(G)

The Lord detests all the proud of heart.(H)
    Be sure of this: They will not go unpunished.(I)

Through love and faithfulness sin is atoned for;
    through the fear of the Lord(J) evil is avoided.(K)

When the Lord takes pleasure in anyone’s way,
    he causes their enemies to make peace(L) with them.(M)

Better a little with righteousness
    than much gain(N) with injustice.(O)

In their hearts humans plan their course,
    but the Lord establishes their steps.(P)

10 The lips of a king speak as an oracle,
    and his mouth does not betray justice.(Q)

11 Honest scales and balances belong to the Lord;
    all the weights in the bag are of his making.(R)

12 Kings detest wrongdoing,
    for a throne is established through righteousness.(S)

13 Kings take pleasure in honest lips;
    they value the one who speaks what is right.(T)

14 A king’s wrath is a messenger of death,(U)
    but the wise will appease it.(V)

15 When a king’s face brightens, it means life;(W)
    his favor is like a rain cloud in spring.(X)

16 How much better to get wisdom than gold,
    to get insight(Y) rather than silver!(Z)

17 The highway of the upright avoids evil;
    those who guard their ways preserve their lives.(AA)

18 Pride(AB) goes before destruction,
    a haughty spirit(AC) before a fall.(AD)

19 Better to be lowly in spirit along with the oppressed
    than to share plunder with the proud.

20 Whoever gives heed to instruction prospers,[a](AE)
    and blessed is the one who trusts in the Lord.(AF)

21 The wise in heart are called discerning,
    and gracious words promote instruction.[b](AG)

22 Prudence is a fountain of life to the prudent,(AH)
    but folly brings punishment to fools.

23 The hearts of the wise make their mouths prudent,(AI)
    and their lips promote instruction.[c](AJ)

24 Gracious words are a honeycomb,(AK)
    sweet to the soul and healing to the bones.(AL)

25 There is a way that appears to be right,(AM)
    but in the end it leads to death.(AN)

26 The appetite of laborers works for them;
    their hunger drives them on.

27 A scoundrel(AO) plots evil,
    and on their lips it is like a scorching fire.(AP)

28 A perverse person stirs up conflict,(AQ)
    and a gossip separates close friends.(AR)

29 A violent person entices their neighbor
    and leads them down a path that is not good.(AS)

30 Whoever winks(AT) with their eye is plotting perversity;
    whoever purses their lips is bent on evil.

31 Gray hair is a crown of splendor;(AU)
    it is attained in the way of righteousness.

32 Better a patient person than a warrior,
    one with self-control than one who takes a city.

33 The lot is cast(AV) into the lap,
    but its every decision(AW) is from the Lord.(AX)

Footnotes

  1. Proverbs 16:20 Or whoever speaks prudently finds what is good
  2. Proverbs 16:21 Or words make a person persuasive
  3. Proverbs 16:23 Or prudent / and make their lips persuasive