Add parallel Print Page Options

27 Usamanyadire za mawa,
    pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.

Munthu wina akutamande, koma osati wekha;
    mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.

Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri,
    koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.

Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa.
    Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.

Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino
    kuposa chikondi chobisika.

Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino,
    koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.

Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi,
    koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.

Munthu amene wasochera ku nyumba kwake,
    ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.

Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima,
    ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.

10 Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako,
    ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto;
    mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.

11 Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga;
    pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.

12 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,
    koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.

13 Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;
    ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.

14 Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri,
    anthu adzamuyesa kuti akutemberera.

15 Mkazi wolongolola ali ngati
    mvula yamvumbi.
16 Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo
    kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.

17 Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake,
    chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.

18 Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake,
    ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.

19 Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi,
    chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.

20 Manda sakhuta,
    nawonso maso a munthu sakhuta.

21 Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo,
    chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.

22 Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo
    ndi musi ngati chimanga,
    uchitsiru wakewo sudzachoka.

23 Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili.
    Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 Paja chuma sichikhala mpaka muyaya,
    ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Pamene udzu watha, msipu nʼkumera;
    ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 ana ankhosa adzakupatsani chovala
    ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri
    kuti muzidya inuyo ndi banja lanu
    ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

27 Do not boast(A) about tomorrow,
    for you do not know what a day may bring.(B)

Let someone else praise you, and not your own mouth;
    an outsider, and not your own lips.(C)

Stone is heavy and sand(D) a burden,
    but a fool’s provocation is heavier than both.

Anger is cruel and fury overwhelming,
    but who can stand before jealousy?(E)

Better is open rebuke
    than hidden love.

Wounds from a friend can be trusted,
    but an enemy multiplies kisses.(F)

One who is full loathes honey from the comb,
    but to the hungry even what is bitter tastes sweet.

Like a bird that flees its nest(G)
    is anyone who flees from home.

Perfume(H) and incense bring joy to the heart,
    and the pleasantness of a friend
    springs from their heartfelt advice.

10 Do not forsake your friend or a friend of your family,
    and do not go to your relative’s house when disaster(I) strikes you—
    better a neighbor nearby than a relative far away.

11 Be wise, my son, and bring joy to my heart;(J)
    then I can answer anyone who treats me with contempt.(K)

12 The prudent see danger and take refuge,
    but the simple keep going and pay the penalty.(L)

13 Take the garment of one who puts up security for a stranger;
    hold it in pledge if it is done for an outsider.(M)

14 If anyone loudly blesses their neighbor early in the morning,
    it will be taken as a curse.

15 A quarrelsome wife is like the dripping(N)
    of a leaky roof in a rainstorm;
16 restraining her is like restraining the wind
    or grasping oil with the hand.

17 As iron sharpens iron,
    so one person sharpens another.

18 The one who guards a fig tree will eat its fruit,(O)
    and whoever protects their master will be honored.(P)

19 As water reflects the face,
    so one’s life reflects the heart.[a]

20 Death and Destruction[b] are never satisfied,(Q)
    and neither are human eyes.(R)

21 The crucible for silver and the furnace for gold,(S)
    but people are tested by their praise.

22 Though you grind a fool in a mortar,
    grinding them like grain with a pestle,
    you will not remove their folly from them.

23 Be sure you know the condition of your flocks,(T)
    give careful attention to your herds;
24 for riches do not endure forever,(U)
    and a crown is not secure for all generations.
25 When the hay is removed and new growth appears
    and the grass from the hills is gathered in,
26 the lambs will provide you with clothing,
    and the goats with the price of a field.
27 You will have plenty of goats’ milk to feed your family
    and to nourish your female servants.

Footnotes

  1. Proverbs 27:19 Or so others reflect your heart back to you
  2. Proverbs 27:20 Hebrew Abaddon