Add parallel Print Page Options

28 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,
    koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,
    koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake
    ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,
    koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,
    koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

Munthu wosauka wa makhalidwe abwino
    aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,
    koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka
    amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

Wokana kumvera malamulo
    ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa
    adzagwera mu msampha wake womwe,
    koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,
    koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;
    koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,
    koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,
    koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa
    ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza
    koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu
    adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;
    wina aliyense asamuthandize.

18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa
    koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,
    koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,
    koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21 Kukondera si kwabwino,
    ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera
    koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake
    mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake
    namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”
    ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano,
    koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,
    koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,
    koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,
    koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

28 The wicked flee(A) though no one pursues,(B)
    but the righteous are as bold as a lion.(C)

When a country is rebellious, it has many rulers,
    but a ruler with discernment and knowledge maintains order.

A ruler[a] who oppresses the poor
    is like a driving rain that leaves no crops.

Those who forsake instruction praise the wicked,
    but those who heed it resist them.

Evildoers do not understand what is right,
    but those who seek the Lord understand it fully.

Better the poor whose walk is blameless
    than the rich whose ways are perverse.(D)

A discerning son heeds instruction,
    but a companion of gluttons disgraces his father.(E)

Whoever increases wealth by taking interest(F) or profit from the poor
    amasses it for another,(G) who will be kind to the poor.(H)

If anyone turns a deaf ear to my instruction,
    even their prayers are detestable.(I)

10 Whoever leads the upright along an evil path
    will fall into their own trap,(J)
    but the blameless will receive a good inheritance.

11 The rich are wise in their own eyes;
    one who is poor and discerning sees how deluded they are.

12 When the righteous triumph, there is great elation;(K)
    but when the wicked rise to power, people go into hiding.(L)

13 Whoever conceals their sins(M) does not prosper,
    but the one who confesses(N) and renounces them finds mercy.(O)

14 Blessed is the one who always trembles before God,
    but whoever hardens their heart falls into trouble.

15 Like a roaring lion or a charging bear
    is a wicked ruler over a helpless people.

16 A tyrannical ruler practices extortion,
    but one who hates ill-gotten gain will enjoy a long reign.

17 Anyone tormented by the guilt of murder
    will seek refuge(P) in the grave;
    let no one hold them back.

18 The one whose walk is blameless is kept safe,(Q)
    but the one whose ways are perverse will fall(R) into the pit.[b]

19 Those who work their land will have abundant food,
    but those who chase fantasies will have their fill of poverty.(S)

20 A faithful person will be richly blessed,
    but one eager to get rich will not go unpunished.(T)

21 To show partiality(U) is not good(V)
    yet a person will do wrong for a piece of bread.(W)

22 The stingy are eager to get rich
    and are unaware that poverty awaits them.(X)

23 Whoever rebukes a person will in the end gain favor
    rather than one who has a flattering tongue.(Y)

24 Whoever robs their father or mother(Z)
    and says, “It’s not wrong,”
    is partner to one who destroys.(AA)

25 The greedy stir up conflict,(AB)
    but those who trust in the Lord(AC) will prosper.

26 Those who trust in themselves are fools,(AD)
    but those who walk in wisdom are kept safe.(AE)

27 Those who give to the poor will lack nothing,(AF)
    but those who close their eyes to them receive many curses.(AG)

28 When the wicked rise to power, people go into hiding;(AH)
    but when the wicked perish, the righteous thrive.

Footnotes

  1. Proverbs 28:3 Or A poor person
  2. Proverbs 28:18 Syriac (see Septuagint); Hebrew into one