Add parallel Print Page Options

Mawu a Mfumu Lemueli

31 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:

Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga?
    Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Usapereke mphamvu yako kwa akazi.
    Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.

Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu,
    mafumu sayenera kumwa vinyo.
    Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko,
    nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa,
    vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
amwe kuti ayiwale umphawi wawo
    asakumbukirenso kuvutika kwawo.

Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.
    Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo.
    Uwateteze amphawi ndi osauka.

Mathero: Mkazi Wangwiro

10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?
    Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira
    ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Masiku onse a moyo wake
    mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;
    amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,
    amakatenga chakudya chake kutali.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni;
    ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya
    ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;
    ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Iye amavala zilimbe
    nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,
    choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Iye amadzilukira thonje
    ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka
    ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu;
    pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake;
    amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda,
    ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;
    amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;
    ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Iye amayankhula mwanzeru,
    amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake
    ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala;
    ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana
    koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;
    koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita
    ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

Sayings of King Lemuel

31 The sayings(A) of King Lemuel—an inspired utterance his mother taught him.

Listen, my son! Listen, son of my womb!
    Listen, my son, the answer to my prayers!(B)
Do not spend your strength[a] on women,
    your vigor on those who ruin kings.(C)

It is not for kings, Lemuel—
    it is not for kings to drink wine,(D)
    not for rulers to crave beer,
lest they drink(E) and forget what has been decreed,(F)
    and deprive all the oppressed of their rights.
Let beer be for those who are perishing,
    wine(G) for those who are in anguish!
Let them drink(H) and forget their poverty
    and remember their misery no more.

Speak(I) up for those who cannot speak for themselves,
    for the rights of all who are destitute.
Speak up and judge fairly;
    defend the rights of the poor and needy.(J)

Epilogue: The Wife of Noble Character

10 [b]A wife of noble character(K) who can find?(L)
    She is worth far more than rubies.
11 Her husband(M) has full confidence in her
    and lacks nothing of value.(N)
12 She brings him good, not harm,
    all the days of her life.
13 She selects wool and flax
    and works with eager hands.(O)
14 She is like the merchant ships,
    bringing her food from afar.
15 She gets up while it is still night;
    she provides food for her family
    and portions for her female servants.
16 She considers a field and buys it;
    out of her earnings she plants a vineyard.
17 She sets about her work vigorously;
    her arms are strong for her tasks.
18 She sees that her trading is profitable,
    and her lamp does not go out at night.
19 In her hand she holds the distaff
    and grasps the spindle with her fingers.
20 She opens her arms to the poor
    and extends her hands to the needy.(P)
21 When it snows, she has no fear for her household;
    for all of them are clothed in scarlet.
22 She makes coverings for her bed;
    she is clothed in fine linen and purple.
23 Her husband is respected at the city gate,
    where he takes his seat among the elders(Q) of the land.
24 She makes linen garments and sells them,
    and supplies the merchants with sashes.
25 She is clothed with strength and dignity;
    she can laugh at the days to come.
26 She speaks with wisdom,
    and faithful instruction is on her tongue.(R)
27 She watches over the affairs of her household
    and does not eat the bread of idleness.
28 Her children arise and call her blessed;
    her husband also, and he praises her:
29 “Many women do noble things,
    but you surpass them all.”
30 Charm is deceptive, and beauty is fleeting;
    but a woman who fears the Lord is to be praised.
31 Honor her for all that her hands have done,
    and let her works bring her praise(S) at the city gate.

Footnotes

  1. Proverbs 31:3 Or wealth
  2. Proverbs 31:10 Verses 10-31 are an acrostic poem, the verses of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.