Add parallel Print Page Options

Miyambo ya Solomoni

10 Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,
    koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,
    koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;
    koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

Wochita zinthu mwaulesi amasauka,
    koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,
    koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,
    koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,
    koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,
    koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;
    koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,
    koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,
    koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12 Udani umawutsa mikangano,
    koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,
    koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14 Anzeru amasunga chidziwitso
    koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15 Chuma cha munthu wolemera
    ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,
    koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,
    koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,
    ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,
    koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,
    koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;
    koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,
    ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,
    koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;
    chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,
    koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,
    ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;
    koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,
    koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,
    koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake
    koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,
    koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,
    koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.